< Yoswa 13 >

1 Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
A Isus veæ bijaše star i vremenit. I reèe mu Gospod: ti si star i vremenit, a zemlje je ostalo vrlo mnogo da se osvoji.
2 “Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
Ovo je zemlja što je ostala: sve meðe Filistejske i sva Gesurska,
3 kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
Od Siora, koji je pred Misirom, do meðe Akaronske na sjever; to pripada Hananejima; pet kneževina Filistejskih, Gazejska, Azotska, Askalonska, Getejska i Akaronska, i Aveji;
4 Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
S juga sva zemlja Hananejska i Meara, što pripada Sidoncima do Afeka, do meðe Amorejske.
5 Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
I zemlja Givlejska i sav Livan k istoku, od Val-Gada pod gorom Ermonom pa do ulaska Ematskoga;
6 “Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
Sve koji žive u toj gori od Livana do vode Misrefota, sve Sidonce ja æu otjerati ispred sinova Izrailjevih; samo je razdijeli ždrijebom Izrailju u našljedstvo, kao što sam ti zapovjedio.
7 Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
Razdijeli dakle tu zemlju u našljedstvo meðu devet plemena i polovinu plemena Manasijina.
8 Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
Jer s drugom polovinom pleme Ruvimovo i Gadovo primiše svoj dio, koji im dade Mojsije s onu stranu Jordana k istoku, kako im dade Mojsije sluga Gospodnji,
9 Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
Od Aroira koji je na brijegu potoka Arnona i grada nasred potoka, i svu ravnicu Medevsku do Devona,
10 Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
I sve gradove Siona cara Amorejskoga, koji careva u Esevonu, do meðe sinova Amonovijeh,
11 Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
I Galad i meðu Gesursku i Mahatsku i svu goru Ermonsku i sav Vasan do Salhe;
12 Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
Sve carstvo Ogovo u Vasanu, koji Og carova u Astarotu i Edrajinu i bješe ostao od Rafaja; a Mojsije ih pobi i istrijebi.
13 Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
Ali Gesureja i Mahateja ne izagnaše sinovi Izrailjevi, nego Gesureji i Mahateji ostaše meðu Izrailjem do danas.
14 Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
Samo plemenu Levijevu ne dade našljedstva; žrtve ognjene Gospoda Boga Izrailjeva jesu našljedstvo njegovo, kao što mu je rekao.
15 Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
A dade Mojsije plemenu sinova Ruvimovijeh po porodicama njihovijem,
16 Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
I meðe im bjehu od Aroira koji je na brijegu potoka Arnona, i grad koji je na srijedi potoka, i sva ravan do Medeve,
17 Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
Esevon sa svijem gradovima svojim u ravni, Devon i Vamot-Val i Vet-Valmeon,
18 Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
I Jasa i Kadimot i Mifat,
19 Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
I Kirijatajim i Sivma i Zaret-Sar na gori kod doline,
20 Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
I Vet-Fegor i Azdot-Fazga i Vet-Jesimot,
21 Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
I svi gradovi u ravni, i sve carstvo Siona cara Amorejskoga, koji carova u Esevonu, kojega ubi Mojsije s knezovima Madijamskim, Evijom i Rekemom i Surom i Urom i Revom, knezovima Sionovijem, koji življahu u onoj zemlji.
22 Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
I Valama sina Veorova vraèa ubiše sinovi Izrailjevi maèem s drugima pobijenijem.
23 Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
I bjehu meðe sinova Ruvimovijeh Jordan s meðama svojim. To je našljedstvo sinova Ruvimovijeh po porodicama njihovijem, gradovi i sela njihova.
24 Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
I dade Mojsije plemenu Gadovu, sinovima Gadovijem po porodicama njihovijem,
25 Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
I bjehu im meðe Jazir i svi gradovi Galadski i polovina zemlje sinova Amonovijeh do Aroira koji je prema Ravi,
26 ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
I od Esevona do Ramot-Mispe i Vetonima, i od Mahanaima do meðe Davirske;
27 Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
I u dolini Vet-Aram i Vet-Nimra i Sokot i Safon; ostatak carstva Siona cara Esevonskoga, Jordan i meða njegova do kraja mora Hinerotskoga s onu stranu Jordana na istok.
28 Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
To je našljedstvo sinova Gadovijeh po porodicama njihovijem, gradovi i sela njihova.
29 Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
I dade Mojsije polovini plemena Manasijina, i dobi polovina plemena sinova Manasijinih po porodicama svojim;
30 Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
Meða im bješe od Mahanaima, sav Vasan, sve carstvo Oga cara Vasanskoga, i sva sela Jairova, što su u Vasanu, šezdeset gradova.
31 Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
I polovina Galada, i Astarot i Edrajin, gradovi carstva Ogova u Vasanu, dopadoše sinovima Mahira sina Manasijina, polovini sinova Mahirovijeh po porodicama njihovijem.
32 Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
To je što razdijeli u našljedstvo Mojsije u polju Moavskom s onu stranu Jordana prema Jerihonu na istoku.
33 Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.
A plemenu Levijevu ne dade Mojsije našljedstva; Gospod je Bog Izrailjev njihovo našljedstvo, kao što im je rekao.

< Yoswa 13 >