< Yeremiya 20 >

1 Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi.
A Pashor sin Imirov sveštenik, koji bijaše starješina u domu Gospodnjem, èu Jeremiju gdje prorokuje te rijeèi.
2 Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova.
I udari Pashor proroka Jeremiju, i metnu ga u tamnicu na gornjim vratima Venijaminovijem uz dom Gospodnji.
3 Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse.
A sjutradan kad Pashor izvede Jeremiju iz tamnice, reèe mu Jeremija: Gospod ti nadje ime ne Pashor nego Magor-Misaviv.
4 Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo.
Jer ovako veli Gospod: evo, ja æu pustiti na te strah, na te i na sve prijatelje tvoje, koji æe pasti od maèa neprijatelja svojih, i oèi æe tvoje vidjeti, i svega æu Judu dati u ruke caru Vavilonskom, koji æe ih odvesti u Vavilon, i pobiæe ih maèem.
5 Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni.
I daæu sve bogatstvo toga grada i sav trud njegov i sve što ima dragocjeno, i sve blago careva Judinijeh daæu neprijateljima njihovijem u ruke, i razgrabiæe i uzeti i odnijeti u Vavilon.
6 Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’”
I ti, Pashore, i svi koji žive u tvom domu otiæi æete u ropstvo; i doæi æeš u Vavilon i ondje æeš umrijeti i ondje æeš biti pogreben ti i svi prijatelji tvoji, kojima si prorokovao lažno.
7 Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi; Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana. Anthu akundinyoza tsiku lonse. Aliyense akundiseka kosalekeza.
Nagovarao si me, Gospode, i dadoh se nagovoriti; bio si jaèi od mene i nadvladao si me; na potsmijeh sam svaki dan, svak mi se potsmijeva.
8 Nthawi iliyonse ndikamayankhula, ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka! Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.
Jer otkad govorim, vapijem, radi nasilja i pustošenja vièem, jer mi je rijeè Gospodnja na porugu i na potsmijeh svaki dan.
9 Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,” mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga, amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga. Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa, koma sindingathe kupirirabe.
I rekoh: neæu ga više pominjati, niti æu više govoriti u ime njegovo; ali bi u srcu mom kao oganj razgorio, zatvoren u kostima mojim, i umorih se zadržavajuæi ga, i ne mogoh više.
10 Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti, “Zoopsa ku mbali zonse! Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!” Onse amene anali abwenzi anga akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti, “Mwina mwake adzanyengedwa; tidzamugwira ndi kulipsira pa iye.”
Jer èujem poruge od mnogih, strah otsvuda: prokažite da prokažemo; svi koji bijahu u miru sa mnom, vrebaju da posrnem: da ako se prevari, te æemo ga nadvladati i osvetiæemo mu se.
11 Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu. Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana. Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana. Manyazi awo sadzayiwalika konse.
Ali je Gospod sa mnom kao strašan junak; zato oni koji me gone spotaknuæe se i neæe nadvladati; posramiæe se vrlo; jer neæe biti sreæni, sramota vjeèna neæe se zaboraviti.
12 Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu. Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.
Zato, Gospode nad vojskama, koji kušaš pravednika, koji vidiš bubrege i srce, daj da vidim tvoju osvetu na njima, jer tebi kazah parbu svoju.
13 Imbirani Yehova! Mutamandeni Yehova! Iye amapulumutsa wosauka mʼmanja mwa anthu oyipa.
Pjevajte Gospodu, hvalite Gospoda, jer izbavi dušu siromahu iz ruke zlikovaèke.
14 Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa! Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!
Proklet da je dan u koji se rodih! dan, u koji me rodi mati moja, da nije blagosloven!
15 Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga ndi uthenga woti: “Kwabadwa mwana wamwamuna!”
Proklet da je èovjek koji javi ocu mojemu i vrlo ga obradova govoreæi: rodi ti se sin.
16 Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene Yehova anayiwononga mopanda chisoni. Amve mfuwu mmawa, phokoso la nkhondo masana.
I taj èovjek da bi bio kao gradovi koje Gospod zatr i ne bi mu žao! neka sluša viku ujutru i vrisku u podne,
17 Chifukwa sanandiphere mʼmimba, kuti amayi anga asanduke manda anga, mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.
Što me ne usmrti u utrobi materinoj da bi mi mati moja bila grob, i utroba njezina da bi ostala dovijeka trudna.
18 Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni kuti moyo wanga ukhale wamanyazi wokhawokha?
Zašto izidoh iz utrobe da vidim muku i žalost i da se svrše u sramoti dani moji?

< Yeremiya 20 >