< Yeremiya 21 >

1 Mfumu Zedekiya inatuma Pasuri mwana wa Malikiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa Yeremiya.
Rijeè koja doðe Jeremiji od Gospoda kad posla k njemu car Sedekija Pashora sina Melhijina i Sofoniju sina Masijina sveštenika, i poruèi:
2 Iwo amati akanene kwa Yeremiya mawu akuti, “Tinenere kwa Yehova chifukwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni akutithira nkhondo. Mwina mwake Yehova nʼkutichitira zodabwitsa kuti Nebukadinezarayo achoke kwathu kuno.”
Upitaj Gospoda za nas, jer Navuhodonosor car Vavilonski zavojšti na nas; eda bi nam uèinio Gospod po svijem èudesima svojim, da otide od nas.
3 Koma Yehova anawuza Yeremiya kuti ayankhe Pasuri ndi Zefaniya kuti, “Kamuwuzeni Zedekiya kuti,
A Jeremija im reèe: ovako recite Sedekiji:
4 ‘Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ndikulandeni zida zimene zili mʼmanja mwanu zimene mukugwiritsa ntchito polimbana ndi mfumu ya ku Babuloni ndi ankhondo ake amene akuzingani kunja kwa lingali. Ndipo ndidzasonkhanitsa zidazo mʼkati mwa mzindawu.
Ovako veli Gospod Bog Izrailjev: evo, ja æu okrenuti natrag oružje što je u vašim rukama, kojim se bijete s carem Vavilonskim i s Haldejcima koji su vas opkolili iza zidova, i skupiæu ih usred toga grada.
5 Ineyo mwini wakene ndi mkono wotambasula ndi dzanja lamphamvu, ndidzachita nanu nkhondo ndili wokwiya, wokalipa ndi waukali.
I ja æu vojevati na vas rukom podignutom i mišicom krjepkom i gnjevom i jarošæu i žestinom velikom.
6 Ndidzakantha amene amakhala mu mzinda muno, anthu pamodzi ndi zirombo, ndipo zidzafa ndi mliri woopsa.
I pobiæu stanovnike toga grada, i ljude i stoku; od pomora velikoga pomrijeæe.
7 Pambuyo pake, ndidzapereka Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi anthu a mu mzinda muno amene adzapulumuke pa nthawi ya mliri, lupanga ndi njala kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi kwa adani awo amene ankafuna kuwapha. Iye adzawapha ndi lupanga. Sadzawachitira chifundo kapena kuwamvera chisoni kapenanso kuwakomera mtima.’
A poslije, veli Gospod, daæu Sedekiju cara Judina i sluge njegove i narod, one koji ostanu u tom gradu od pomora, od maèa i od gladi, u ruke Navuhodonosoru caru Vavilonskom i u ruke neprijateljima njihovijem i u ruke onima koji traže dušu njihovu, te æe ih pobiti maèem, neæe ih žaliti ni štedjeti niti æe se smilovati.
8 “Yehova anati ndiwawuzenso anthu amenewa kuti asankhe pakati pa moyo ndi imfa.
A narodu tome reci: ovako veli Gospod: evo ja stavljam pred vas put k životu i put k smrti.
9 Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzaphedwa ndi lupanga, njala kapena mliri. Koma aliyense amene apite kukadzipereka kwa Ababuloni amene akuzinganiwa adzakhala ndi moyo, adzapulumuka.
Ko ostane u tom gradu, poginuæe od maèa ili od gladi ili od pomora; a ko izaðe i preda se Haldejcima koji su vas opkolili, ostaæe živ, i duša æe mu biti mjesto plijena.
10 Ine ndatsimikiza kuchitira mzinda uno choyipa osati chabwino, akutero Yehova. Udzaperekedwa mʼdzanja la mfumu ya ku Babuloni, ndipo iyeyo adzawutentha ndi moto.
Jer okretoh lice svoje tome gradu na zlo a ne na dobro, govori Gospod; u ruke caru Vavilonskom biæe predan, i on æe ga spaliti ognjem.
11 “Komanso, uwuze banja laufumu la Yuda kuti, ‘Imva mawu a Yehova;
A za dom cara Judina èujte rijeè Gospodnju:
12 inu a mʼbanja la Davide, Yehova akuti, “‘Weruzani mwachilungamo mmawa uliwonse; pulumutsani mʼdzanja la wozunza aliyense amene walandidwa katundu wake, kuopa kuti ukali wanga ungabuke ndi kuyaka ngati moto wosazimitsika chifukwa cha zoyipa zimene mwachita.
Dome Davidov, tako veli Gospod, sudite svako jutro, i kome se otima izbavljajte ga iz ruku nasilnikovijeh da ne izaðe kao oganj gnjev moj i razgori se da ga niko ne može ugasiti za zloæu djela vaših.
13 Ndidzalimbana nanu, inu amene mukukhala pamwamba pa chigwa, inu okhala ngati thanthwe lapachidikha, akutero Yehova. Inu amene mumanena kuti, ‘Ndani amene angabwere kudzalimbana nafe? Ndani amene angathe kulowa mʼmalinga mwathu?’
Evo me na tebe, koji sjediš u dolini, kao stijena u ravnici, govori Gospod, na vas, koji govorite: ko æe doæi na nas? i ko æe uæi u stanove naše?
14 Ndidzakulangani molingana ndi ntchito zanu, akutero Yehova. Ndidzatentha nkhalango zanu; moto udzapsereza zonse zimene zakuzungulirani.’”
Jer æu vas pokarati po plodu djela vaših, veli Gospod, i raspaliæu oganj u šumi njegovoj, koji æe proždrijeti sve što je oko njega.

< Yeremiya 21 >