< Yeremiya 19 >

1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukagule mʼphika wadothi kwa munthu wowumba. Utenge akuluakulu ena a anthuwa ndi ansembe
Ovako reèe Gospod: idi i kupi krèag zemljan u lonèara s nekoliko starješina narodnijeh i starješina sveštenièkih.
2 ndipo mupite ku Chigwa cha Hinomu chimene chili pafupi ndi pa chipata cha mapale. Pamenepo ukalengeze mawu amene ndikakuwuze.
I otidi u dolinu sina Enomova što je pred vratima istoènijem, i ondje proglasi rijeèi koje æu ti kazati.
3 Ukanene kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu a ku Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu. Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti: Tamverani! Ine ndibweretsa mavuto pa malo pano mwakuti aliyense amene adzamve adzadzidzimuka.
I reci: èujte rijeè Gospodnju, carevi Judini i stanovnici Jerusalimski; ovako veli Gospod nad vojskama Bog Izrailjev: evo, ja æu pustiti zlo na to mjesto da æe zujati uši svakome ko ga èuje.
4 Pakuti anthu andikana Ine ndipo ayipitsa malo ano. Afukiza lubani pa malo ano kwa milungu imene iwo ngakhale makolo awo ngakhalenso mafumu a ku Yuda sanayidziwe. Iwo adzaza malowa ndi magazi a anthu osalakwa.
Jer me ostaviše i oskvrniše ovo mjesto kadeæi na njemu drugim bogovima, kojih ne znaše ni oni ni oci njihovi, ni carevi Judini, i napuniše to mjesto krvi prave.
5 Amanga nsanja zopembedzerapo Baala, kuperekapo ana awo kuti akhale nsembe zopsereza kwa Baala, chinthu chimene Ine sindinalamule kapena kuchiyankhula, ngakhalenso kuchiganizira.
I pogradiše visine Valu da sažižu sinove svoje ognjem na žrtve paljenice Valu, èega ne zapovjedih niti o tom govorih, niti mi na um doðe.
6 Nʼchifukwa chake taonani, masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzatchulanso malo ano kuti Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma Chophera anthu.
Zato, evo, ide vrijeme, veli Gospod, kad se ovo mjesto neæe više zvati Tofet, ni dolina sina Enomova, nego krvna dolina.
7 “‘Pamalo pano ndidzasokoneza maganizo a anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. Ndidzachititsa kuti adani awo awaphe ku nkhondo. Ndidzawakanthitsa kwa anthu amene akuwazonda. Mitembo yawo ndidzayipereka kwa mbalame za mlengalenga ndi zirombo za kutchire kuti ikhale chakudya chawo.
Jer æu uništiti savjet Judin i Jerusalimski na ovom mjestu, i uèiniæu da padnu od maèa pred neprijateljima svojim i od ruke onijeh koji traže dušu njihovu, i mrtva æu tjelesa njihova dati za hranu pticama nebeskim i zvijerima zemaljskim.
8 Mzinda uno ndidzawusakaza ndi kuwusandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyansa. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
I obratiæu taj grad u pustoš i rug: ko god proðe mimo nj, èudiæe se i zviždaæe za sve muke njegove.
9 Adani awo adzawuzinga mzindawo kufuna kuwapha motero kuti anthu a mʼkatimo adzafika pomadyana wina ndi mnzake. Adzadya ana awo aamuna ndi ana awo aakazi.’
I uèiniæu da jedu meso od svojih sinova i meso od svojih kæeri, i svaki æe jesti meso od druga svojega u nevolji i tjeskobi kojom æe im dosaðivati neprijatelji njihovi i koji traže dušu njihovu.
10 “Tsono iwe udzaphwanye mtsukowo anthu amene udzapite nawowo akuona,
Potom razbij krèag pred ljudima koji æe iæi s tobom.
11 ndipo ukawawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndidzaphwanya dziko lino ndi mzinda uno ngati momwe wowumba amaphwanyira mbiya yake ndipo sangathe kuyikonzanso. Adzayika anthu akufa ku Tofeti chifukwa padzasowa malo ena owayika.
I reci im: ovako veli Gospod nad vojskama: tako æu razbiti taj narod i taj grad kao što se razbije sud lonèarski, koji se ne može više opraviti, i u Tofetu æe se pogrebavati, jer neæe biti mjesta za pogrebavanje.
12 Umu ndi mmene ndidzachitire ndi malo ano pamodzi ndi anthu okhalamo, akutero Yehova. Ndidzasandutsa mzindawu kukhala ngati Tofeti.
Tako æu uèiniti tome mjestu, veli Gospod, i stanovnicima njegovijem i uèiniæu taj grad da bude kao Tofet;
13 Nyumba za mu Yerusalemu ndi za mafumu a ku Yuda ndidzazisandutsa ngati za ku Tofeti chifukwa ndi nyumba zimene pa madenga ake ankafukiza lubani kwa zolengedwa zamlengalenga ndi kuthira nsembe zachakumwa kwa milungu ina.’”
I kuæe Jerusalimske i kuæe careva Judinijeh biæe neèiste kao mjesto Tofet, sve kuæe, gdje na krovovima kadiše svoj vojsci nebeskoj i ljevaše naljeve drugim bogovima.
14 Kenaka Yeremiya anabwerako ku Tofeti, kumene Yehova anamutuma kuti akanenere, nakayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Yehova ndi kuwawuza anthu kuti,
Potom se vrati Jeremija iz Tofeta kuda ga bješe poslao Gospod da prorokuje, i stade u trijemu doma Gospodnjega, i reèe svemu narodu:
15 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Tamverani! Ine ndidzabweretsa masautso amene ndinanena aja pa mzinda uno ndi pa mizinda yozungulira, chifukwa anthu ake ndi nkhutukumve ndipo sanamvere mawu anga.’”
Ovako veli Gospod nad vojskama Bog Izrailjev: evo, ja æu pustiti na taj grad i na sve gradove njegove sve zlo koje izrekoh za nj, jer otvrdnuše vratom svojim da ne slušaju rijeèi mojih.

< Yeremiya 19 >