< Yesaya 8 >

1 Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
And the Lord seide to me, Take to thee a greet book, and write ther ynne with the poyntil of man, Swiftli drawe thou awei spuylis, take thou prey soone.
2 Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
And Y yaf to me faithful witnessis, Vrie, the prest, and Sacarie, the sone of Barachie.
3 Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
And Y neiyede to the profetesse; and sche conseyuede, and childide a sone. And the Lord seide to me, Clepe thou his name Haste thou to drawe awei spuylis, haaste thou for to take prey.
4 Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
For whi bifor that the child kan clepe his fadir and his modir, the strengthe of Damask schal be doon awei, and the spuylis of Samarie, bifor the kyng of Assiriens.
5 Yehova anayankhulanso ndi Ine;
And the Lord addide to speke yit to me, and he seide,
6 “Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
For that thing that this puple hath caste awei the watris of Siloe, that goen with silence, and hath take more Rasyn, and the sone of Romelie, for this thing lo!
7 nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
the Lord schal brynge on hem the stronge and many watris of the flood, the king of Assiriens, and al his glorie; and he schal stiye on alle the stremes therof, and he schal flowe on alle the ryueris therof.
8 Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
And he schal go flowynge bi Juda, and he schal passe til to the necke, and schal come; and the spredyng forth of hise wyngis schal be, and schal fille the breede of thi lond, thou Emanuel.
9 Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
Puplis, be ye gaderid togidere, and be ye ouercomun; and alle londis afer, here ye. Be ye coumfortid, and be ye ouercomun; gird ye you, and be ye ouercomun;
10 Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
take ye councel, and it schal be destried; speke ye a word, and it schal not be doon, for God is with vs.
11 Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
For whi the Lord seith these thingis to me, as he tauyte me in a stronge hond, that Y schulde not go in to the weie of this puple,
12 “Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
and seide, Seie ye not, It is sweryng togidere, for whi alle thingis which this puple spekith is sweryng togidere; and drede ye not the ferdfulnesse therof, nether be ye aferd.
13 Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
Halowe ye the Lord hym silf of oostis; and he schal be youre inward drede, and he schal be youre ferdfulnesse, and he schal be to you in to halewyng.
14 ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
Forsothe he schal be in to a stoon of hirtyng, and in to a stoon of sclaundre, to tweyne housis of Israel; in to a snare, and in to fallyng, to hem that dwellen in Jerusalem.
15 Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
And ful many of hem schulen offende, and schulen falle, and thei schulen be al to-brokun, and thei schulen be boundun, and schulen be takun.
16 Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
Bynde thou witnessyng, mark thou the lawe in my disciplis.
17 Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
Y schal abide the Lord, that hath hid his face fro the hous of Jacob, and Y schal abide hym.
18 Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
Lo! Y and my children, whiche the Lord yaf to me in to a signe, and greet wondur to Israel, of the Lord of oostis that dwellith in the hil of Sion.
19 Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
And whanne thei seien to you, Axe ye of coniureris, and of false dyuynouris, that gnasten in her enchauntyngis, whether the puple schal not axe of her God a reuelacioun for quyke men and deed?
20 kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
It is to go to the lawe more and to the witnessyng, that if thei seien not after this word, morewtide liyt schal not be to hem.
21 Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
And it schal passe bi that, and it schal falle doun, and it schal hungre. And whanne it schal hungre, it schal be wrooth, and schal curse his kyng and his God, and it schal biholde vpward.
22 Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.
And it schal loke to the erthe, and lo! tribulacioun, and derknessis, and vnbyndyng, ether discoumfort, and angwisch, and myist pursuynge; and it schal not mow fle awei fro his angwisch.

< Yesaya 8 >