< Yesaya 9 >

1 Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
In the firste tyme the lond of Zabulon and the lond of Neptalym was releessid; and at the laste the weie of the see biyende Jordan of Galile of hethene men was maad heuy.
2 Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
The puple that yede in derknessis siy a greet liyt; whanne men dwelliden in the cuntre of schadewe of deth, liyt roos vp to hem.
3 Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
Thou multipliedist folk, thou magnefiedist not gladnesse; thei schulen be glad bifore thee, as thei that ben glad in heruest, as ouercomeris maken ful out ioie, whanne thei han take a prey, whanne thei departen the spuylis.
4 Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
For thou hast ouercome the yok of his birthun, and the yerde of his schuldre, and the ceptre of his wrongful axere, as in the day of Madian.
5 Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
For whi al violent raueyn with noise, and a cloth meddlid with blood schal be in to brennyng, and `schal be the mete of fier.
6 Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
Forsothe a litil child is borun to vs, and a sone is youun to vs, and prinsehod is maad on his schuldre; and his name schal be clepid Wondurful, A counselour, God, Strong, A fadir of the world to comynge, A prince of pees.
7 Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
His empire schal be multiplied, and noon ende schal be of his pees; he schal sitte on the seete of Dauid, and on the rewme of hym, that he conferme it, and make stronge in doom and riytfulnesse, fro hennus forth and til in to with outen ende. The feruent loue of the Lord of oostis schal make this.
8 Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
The Lord sente a word in to Jacob, and it felle in Israel.
9 Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
And al the puple of Effraym schal wite, and thei that dwellen in Samarie, seiynge in the pride and greetnesse of herte,
10 “Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
Tijl stoonys fellen doun, but we schulen bilde with square stoonys; thei han kit doun sicomoris, but we schulen chaunge cedris.
11 Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
And the Lord schal reise the enemyes of Rasyn on hym, and he schal turne the enemyes of hym in to noyse;
12 Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
God schal make Sirie to come fro the eest, and Filisteis fro the west; and with al the mouth thei schulen deuoure Israel. In alle these thingis the stronge veniaunce of the Lord is not turned awei, but yit his hond is stretchid forth;
13 Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
and the puple is not turned ayen to the Lord smytynge it, and thei souyten not the Lord of oostis.
14 Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
And the Lord schal leese fro Israel the heed and the tail; crokynge and bischrewynge, ether refreynynge, in o dai.
15 mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
An elde man and onourable, he is the heed, and a profete techynge a leesyng, he is the tail.
16 Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
And thei that blessen his puple, schulen be disseyueris, and thei that ben blessid, schulen be cast doun.
17 Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
For this thing the Lord schal not be glad on the yonge men therof, and he schal not haue merci on the fadirles children and widewis therof; for ech man is an ypocrite and weiward, and ech mouth spak foli. In alle these thingis the stronge veniaunce of hym is not turned awei, but yit his hond is stretchid forth;
18 Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
and the puple is not turned ayen to the Lord smytynge it. For whi wickidnesse is kyndlid as fier; it schal deuoure the breris and thornes, and it schal be kyndlid in the thickenesse of the forest, and it schal be wlappid togidere in the pride of smoke.
19 Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
In the wraththe of the Lord of oostis the lond schal be disturblid, and the puple schal be as the mete of fier; a man schal not spare his brothir.
20 Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
And he schal boowe to the riyt half, and he schal hungre, and he schal ete at the left half, and he schal not be fillid; ech man schal deuoure the fleisch of his arm. Manasses schal deuoure Effraym, and Effraym `schal deuoure Manasses, and thei togidere ayens Juda.
21 Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
In alle these thingis the strong veniaunce of hym is not turned awei, but yit his hoond is stretchid forth.

< Yesaya 9 >