< Yeremiya 1 >

1 Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
The wordis of Jeremye, sone of Helchie, of the preestis that weren in Anathot, in the lond of Beniamyn.
2 Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
For the word of the Lord was maad to hym in the daies of Josie, the sone of Amon, kyng of Juda, in the threttenethe yeer of his rewme.
3 Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
And it was don in the daies of Joachym, the sone of Josie, the king of Juda, til to the endyng of the enleuenthe yeer of Sedechie, sone of Josie, kyng of Juda, til the passyng ouer, ether caitifte, of Jerusalem, in the fyuethe monethe.
4 Yehova anayankhula nane kuti,
And the word of the Lord was maad to me,
5 “Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
and seide, Bifor that Y fourmede thee in the wombe, Y knewe thee; and bifor that thou yedist out of the wombe, Y halewide thee; and Y yaf thee a profete among folkis.
6 Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
And Y seide, A! A! A! Lord God, lo! Y kan not speke, for Y am a child.
7 Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
And the Lord seide to me, Nyle thou seie, that Y am a child; for thou schalt go to alle thingis, to whiche Y schal sende thee, and thou schalt speke alle thingis, what euer thingis Y schal comaunde to thee.
8 Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
Drede thou not of the face of hem, for Y am with thee, to delyuere thee, seith the Lord.
9 Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
And the Lord sente his hond, and touchide my mouth; and the Lord seide to me, Lo! Y haue youe my wordis in thi mouth; lo!
10 Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
Y haue ordeynede thee to day on folkis, and on rewmes, that thou drawe vp, and distrie, and leese, and scatere, and bilde, and plaunte.
11 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
And the word of the Lord was maad to me, and seide, What seest thou, Jeremye?
12 Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
And Y seide, Y se a yerde wakynge. And the Lord seide to me, Thou hast seen wel, for Y schal wake on my word, to do it.
13 Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
And the word of the Lord was maad the secounde tyme to me, and seide, What seest thou? Y se a pot buylynge, and the face therof fro the face of the north.
14 Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
And the Lord seide to me, Fro the north schal be schewid al yuel on alle the dwelleris of the lond.
15 Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
For lo! Y schal clepe togidere alle the naciouns of rewmes of the north, seith the Lord, and thei schulen come, and sette ech man his seete in the entryng of the yatis of Jerusalem, and on alle the wallis therof in cumpas, and on alle the citees of Juda.
16 Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
And Y schal speke my domes with hem on al the malice of hem, that forsoken me, and maden sacrifice to alien goddis, and worschipiden the werk of her hondis.
17 “Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
Therfor girde thou thi leendis, and rise thou, and speke to hem alle thingis whiche Y comaunde to thee; drede thou not of the face of hem, for Y schal not make thee for to drede the cheer of hem.
18 Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
For Y yaf thee to dai in to a strong citee, and in to an yrun piler, and in to a brasun wal, on al the lond, to the kyngis of Juda, and to the princis therof, and to the preestis therof, and to al the puple of the lond.
19 Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
And thei schulen fiyte ayens thee, and thei schulen not haue the maistrie; for Y am with thee, seith the Lord, that Y delyuere thee.

< Yeremiya 1 >