< Yesaya 61 >

1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine, chifukwa Yehova wandidzoza kuti ndilalikire uthenga wabwino kwa anthu osauka. Wandituma kuti ndikatonthoze anthu osweka mtima, ndikalengeze kwa akapolo kuti alandire ufulu ndiponso kuti ndikamasule a mʼndende.
The spirit of the Lord is on me, for the Lord anoyntide me; he sente me to telle to mylde men, that Y schulde heele men contrite in herte, and preche foryyuenesse to caitifs, and openyng to prisoneris; and preche a plesaunt yeer to the Lord,
2 Wandituma kuti ndikalengeze nthawi imene Yehova adzapulumutsa anthu ake; za tsiku limene Yehova adzalanga adani a anthu ake. Wandituma kuti ndikatonthoze olira.
and a dai of veniaunce to oure God; that Y schulde coumforte alle that mourenen;
3 Wandituma kuti ndiwakonzere olira a ku Ziyoni, nkhata ya maluwa yokongola mʼmalo mwa phulusa, ndiwapatse mafuta achikondwerero mʼmalo mwa kulira. Ndiwapatse chovala cha matamando mʼmalo mwa mtima wopsinjika. Ndipo iwo adzatchedwa mitengo ya thundu yamphamvu yachilungamo, yoyidzala Yehova kuti Iye mwini apezemo ulemerero wake.
that Y schulde sette coumfort to the moureneris of Sion, and that Y schulde yyue to them a coroun for aische, oile of ioie for mourenyng, a mentil of preysyng for the spirit of weilyng. And stronge men of riytfulnesse schulen be clepid ther ynne, the plauntyng of the Lord for to glorifie.
4 Adzamanganso mabwinja akale a mzinda ndipo malo amene anawonongeka kalekale aja adzakonzanso. Adzakonzanso mizinda imene inapasuka, imene yakhala yowonongeka kwa nthawi yayitali kwambiri.
And thei schulen bilde thingis `that ben forsakun fro the world, and thei schulen reise elde fallyngis, and thei schulen restore citees `that ben forsakun and distried, in generacioun and in to generacioun.
5 Anthu achilendo adzakutumikirani; adzazidyetsa ziweto zanu; iwo adzagwira ntchito mʼminda yanu ya mpesa.
And aliens schulen stonde, and fede youre beestis; and the sones of pilgrymes schulen be youre erthe tilieris and vyn tilieris.
6 Ndipo inu mudzatchedwa ansembe a Yehova, adzakutchulani kuti ndinu atumiki a Mulungu wathu. Mudzadyerera chuma cha mitundu ya anthu, ndipo mudzanyadira ulemu umene mwalandira.
But ye schulen be clepid the preestis of the Lord; it schal be seid to you, Ye ben mynystris of oure God. Ye schulen ete the strengthe of hethene men, and ye schulen be onourid in the glorie of hem.
7 Chifukwa manyazi awo anali owirikiza; ndi kuti munalandira chitonzo ndi kutukwana, adzakondwera ndi cholowa chawo, tsono adzalandira cholowa chawo cha chigawo cha dziko mowirikiza, ndipo chimwemwe chamuyaya chidzakhala chawo.
For youre double schenschip and schame thei schulen preise the part of hem; for this thing thei schulen haue pesibli double thingis in her lond, and euerlastynge gladnesse schal be to hem.
8 “Pakuti Ine Yehova, ndimakonda chilungamo; ndimadana ndi zakuba ndi zoyipa. Anthu anga ndidzawapatsa mphotho mokhulupirika ndikupangana nawo pangano losatha.
For Y am the Lord, louynge doom, and hatynge raueyn in brent sacrifice. And Y schal yyue the werk of hem in treuthe, and Y schal smyte to hem an euerlastynge boond of pees.
9 Ana awo adzakhala odziwika pakati pa mitundu ya anthu ndipo adzukulu awo adzakhala otchuka pakati pa anthu a mitundu ina. Aliyense wowaona adzazindikira kuti ndi anthu amene Yehova wawadalitsa.”
And the seed of hem schal be knowun among folkis, and the buriownyng of hem in the myddis of puplis. Alle men that seen hem, schulen knowe hem, for these ben the seed, whom the Lord blesside.
10 Ine ndikusangalala kwambiri chifukwa cha Yehova; moyo wanga ukukondwera chifukwa cha Mulungu wanga. Pakuti Iye wandiveka zovala zachipulumutso, ndipo wandiveka mkanjo wachilungamo. Zili ngati mkwati wovala nkhata ya maluwa mʼkhosi mwake, ndiponso ngati mkwatibwi wovala mikanda yamtengowapatali.
I ioiynge schal haue ioie in the Lord, and my soule schal make ful out ioiyng in my God. For he hath clothid me with clothis of helthe, and he hath compassid me with clothis of riytfulnesse, as a spouse made feir with a coroun, and as a spousesse ourned with her brochis.
11 Monga momwe nthaka imameretsa mbewu ndiponso monga munda umakulitsa mbewu zimene anadzala, momwemonso Ambuye Yehova adzaonetsa chilungamo ndi matamando pamaso pa mitundu yonse ya anthu.
For as the erthe bryngith forth his fruyt, and as a gardyn buriowneth his seed, so the Lord God schal make to growe riytfulnesse, and preysyng bifore alle folkis.

< Yesaya 61 >