< Yesaya 60 >

1 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
Rise thou, Jerusalem, be thou liytned, for thi liyt is comun, and the glorie of the Lord is risun on thee.
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
For lo! derknessis schulen hile the erthe, and myist schal hile puplis; but the Lord schal rise on thee, and his glorie schal be seyn in thee.
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
And hethene men schulen go in thi liyt, and kyngis `schulen go in the schynyng of thi risyng.
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
Reise thin iyen in cumpas, and se; alle these men ben gaderid togidere, thei ben comun to thee; thi sones schulen come fro fer, and thi douytris schulen rise fro the side.
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
Thanne thou schalt se, and schalt flowe; and thin herte schal wondre, and schal be alargid, whanne the multitude of the see is conuertid to thee, the strengthe of hethene men is comun to thee;
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
the flowyng of camels schal hile thee, the lederis of dromedis of Madian and of Effa; alle men of Saba schulen come, bryngynge gold and encense, and tellynge heriyng to the Lord.
7 Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
Ech scheep of Cedar schal be gaderid to thee, the rammes of Nabaioth schulen mynystre to thee; thei schulen be offrid on myn acceptable auter, and Y schal glorifie the hous of my maieste.
8 “Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
Who ben these, that fleen as cloudis, and as culueris at her wyndowis?
9 Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
Forsothe ilis abiden me, and the schippis of the see in the bigynnyng; that Y brynge thi sones fro fer, the siluer of hem, and the gold of hem is with hem, to the name of thi Lord God, and to the hooli of Israel; for he schal glorifie thee.
10 “Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
And the sones of pilgrymes schulen bilde thi wallis, and the kyngis of hem schulen mynystre to thee. For Y smoot thee in myn indignacioun, and in my recounselyng Y hadde merci on thee.
11 Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
And thi yatis schulen be openyd contynueli, day and niyt tho schulen not be closid; that the strengthe of hethene men be brouyt to thee, and the kyngis of hem be brouyt.
12 Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
For whi the folk and rewme that serueth not thee, schal perische, and hethene men schulen be distried bi wildirnesse.
13 “Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
The glorie of the Liban schal come to thee, a fir tre, and box tre, and pyne appil tre togidere, to ourne the place of myn halewyng; and Y schal glorifie the place of my feet.
14 Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
And the sones of hem that maden thee lowe, schulen come lowe to thee, and alle that bacbitiden thee, schulen worschipe the steppis of thi feet; and schulen clepe thee A citee of the Lord of Sion, of the hooli of Israel.
15 “Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
For that that thou were forsakun, and hatid, and noon was that passide bi thee, Y schal sette thee in to pryde of worldis, ioie in generacioun and in to generacioun.
16 Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
And thou schalt souke the mylke of folkis, and thou schalt be soclid with the tete of kyngis; and thou schalt wite that Y am the Lord, sauynge thee, and thin ayen biere, the stronge of Jacob.
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
For bras Y schal brynge gold, and for irun Y schal brynge siluer; and bras for trees, and yrun for stoonys; and Y schal sette thi visitacioun pees, and thi prelatis riytfulnesse.
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
Wickidnesse schal no more be herd in thi lond, nether distriyng and defoulyng in thi coostis; and helthe schal ocupie thi wallis, and heriyng schal ocupie thi yatis.
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
The sunne schal no more be to thee for to schyne bi dai, nether the briytnesse of the moone schal liytne thee; but the Lord schal be in to euerlastynge liyt to thee, and thi God schal be in to thi glorie.
20 Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
Thi sunne schal no more go doun, and thi moone schal not be decreessid; for the Lord schal be in to euerlastynge liyt to thee, and the daies of thi mourenyng schulen be fillid.
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
Forsothe thi puple alle iust men, withouten ende schulen enherite the lond, the seed of my plauntyng, the werk of myn hond for to be glorified.
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
The leeste schal be in to a thousynde, and a litil man schal be in to a ful stronge folk. Y, the Lord, schal make this thing sudenli, in the tyme therof.

< Yesaya 60 >