< Ezekieli 40 >

1 Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
In the fyue and twentithe yeer of oure passyng ouer, in the bigynnyng of the yeer, in the tenthe dai of the monethe, in the fourtenthe yeer after that the citee was smytun, in this same dai the hond of the Lord was maad on me, and he brouyte me thidur in the reuelaciouns of God.
2 Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
And he brouyte me in to the lond of Israel, and he leet me doun on a ful hiy hil, on which was as the bildyng of a citee goynge to the south;
3 Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
and he ledde me in thidur. And lo! a man, whos licnesse was as the licnesse of bras, and a coorde of flex was in his hond, and a reed of mesure in his hond; forsothe he stood in the yate.
4 Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
And the same man spak to me, Thou sone of man, se with thin iyen, and here with thin eeris, and sette thin herte on alle thingis, whiche Y schal schewe to thee, for thou art brouyt hidur, that tho be schewid to thee; telle thou alle thingis whiche thou seest to the hous of Israel.
5 Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
And lo! a wal withouteforth, in the cumpas of the hous on ech side; and in the hond of the man was a rehed of mesure of sixe cubitis and a spanne, that is, an handibreede; and he mat the breede of the bildyng with o rehed, and the hiynesse bi o rehed.
6 Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
And he cam to the yate that bihelde the weie of the eest, and he stiede bi degrees of it; and he mat the lyntil of the yate bi o rehed the breede, that is, o lyntil bi o rehed in breede;
7 Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
and he mat o chaumbre bi o rehed in lengthe, and bi o rehed in breed, and fyue cubitis bitwixe chaumbris;
8 Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
and he mat the lyntil of the yate bisidis the porche of the yate with ynne, bi o rehed.
9 Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
And he mat the porch of the yate of eiyte cubitis, and the frount therof bi twei cubitis; sotheli the porche of the yate was with ynne.
10 Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
Certis the chaumbris of the yate at the weie of the eest weren thre on this side, and thre on that side; o mesure of thre, and o mesure of the frountis on euer ethir side.
11 Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
And he mat the breede of the lyntel of the yate of ten cubitis, and the lengthe of the yate of threttene cubitis.
12 Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
And he mat a margyn of a cubit bifor the chaumbris, and o cubit was the ende on ech side; forsothe the chaumbris weren of sixe cubitis on this side and on that side.
13 Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
And he mat the yate fro the roof of the chaumbre til to the roof therof, the breede of fyue and twenti cubitis, a dore ayens a dore.
14 Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
And he made frountes bi sixti cubitis, and at the frount an halle of the yate on ech side bi cumpas;
15 Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
and bifor the face of the yate that stretchith forth til to the face of the porche of the ynner yate, he mat fifti cubitis.
16 Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
And he mat wyndows naraw with out and large with ynne, in the chaumbris and frountis of tho, that weren with ynne the yate on ech side bi cumpas. Sotheli in lijk maner also wyndows weren in the porchis bi cumpas with ynne; and the peynture of palm trees was grauun bifor the frountis.
17 Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
And he ledde me out to the outermere halle, and lo! tresories, and pawment arayed with stoon in the halle bi cumpas; thretti tresories in the cumpas of the pawment;
18 Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
and the pawment was bynethe in the front of the yatis, bi the lengthe of the yatis.
19 Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
And he mat the breede fro the face of the lowere yate til to the frount of the ynnere halle with outforth, an hundrid cubitis at the eest, and at the north.
20 Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
And he mat bothe in lengthe and in breede the yate that bihelde the weie of the north, of the outermore halle.
21 Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
And he mat the chaumbris therof, thre on this side, and thre on that side, and the frount therof, and the porche therof, bi the mesure of the formere yate; the lengthe therof of fifti cubitis, and the breede therof of fyue and twenti cubitis.
22 Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
Sotheli the wyndows therof, and the porche, and the grauyngis, weren bi the mesure of the yate that bihelde to the eest; and the stiyng therof was of seuene degrees, and a porche was bifore it.
23 Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
And the yate of the ynnere halle was ayens the yate of the north, and ayens the eest yate; and he mat fro the yate til to the yate an hundrid cubitis.
24 Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
And he ledde me out to the weie of the south, and lo! the yate that bihelde to the south; and he mat the frount therof, and the porche therof, bi the formere mesuris;
25 Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
and the wyndows therof, and the porchis in cumpas, as othere wyndows; the lengthe of fifti cubitis, and the breede of fyue and twenti cubitis.
26 Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
And bi seuene degrees me stiede to it, and `an halle was bifor the yatis therof; and palme trees weren grauun, oon in this side, and another in that side in the frount therof.
27 Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
And the yate of the ynnere halle was in the weie of the south; and he mat fro the yate til to the yate in the weie of the south, an hundrid cubitis.
28 Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
And he ledde me in to the ynnere halle, to the south yate; and he mat the yate bi the formere mesuris;
29 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
the chaumbre therof, and the frount therof, and the porche therof bi the same mesuris; and he mat the wyndows therof, and the porche therof in cumpas; fifti cubitis of lengthe, and fyue and twenti cubitis of breede.
30 (Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
And he mat the halle bi cumpas, the lengthe of fyue and twenti cubitis, and the breede therof of fyue cubitis.
31 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
And the porche therof was to the outermere halle, and the palm trees therof in the frount; and eiyte degrees weren, bi whiche me stiede thorouy it.
32 Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
And he ledde me in to the ynnere halle, bi the eest weie; and he mat the yate by the formere mesures;
33 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
the chaumbre therof, and the frount therof, and the porchis therof, as aboue; and he mat the wyndows therof, and the porchis therof in cumpas; the lengthe of fifti cubitis, and the breede of fyue and twenti cubitis; and the porche therof,
34 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
that is, of the outermore halle; and palme trees grauun in the frount therof, on this side and on that side; and in eiyte degrees was the stiyng therof.
35 Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
And he ledde me in to the yate that bihelde to the north; and he mat bi the formere mesuris;
36 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
the chaumbre therof, and the frount therof, and the porche therof, and the wyndows therof bi cumpas; the lengthe of fifti cubitis, and the breede of fyue and twenti cubitis.
37 Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
The porche therof bihelde to the outermore halle; and the grauyng of palm trees was in the frount therof, on this side and on that side; and in eiyte degrees was the stiyng therof.
38 Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
And bi alle tresories a dore was in the frountis of yatis; and there thei waischiden brent sacrifice.
39 Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
And in the porche of the yate weren twei boordis on this side, and twei boordis on that side, that brent sacrifice be offrid on tho, `bothe for synne and for trespasse.
40 Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
And at the outermore side, which stieth to the dore of the yate that goith to the north, weren twei boordis; and at `the tother side, bifor the porche of the yate, weren twei boordis.
41 Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
Foure boordis on this side, and foure boordis on that side; bi the sidis of the yate weren eiyte boordis, on whiche thei offriden.
42 Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
Forsothe foure boordis to brent sacrifice weren bildid of square stoonys, in the lengthe of o cubit and an half, and in the breed of o cubit and an half, and in the hiythe of o cubit; on whiche boordis thei schulen sette vessels, in whiche brent sacrifice and slayn sacrifice is offrid.
43 Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
And the brenkis of tho boordis ben of oon handibreede, and ben bowid ayen with ynne bi cumpas; forsothe on the boordis weren fleischis of offryng.
44 Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
And with out the ynnere yate weren tresories of chauntours, in the ynnere halle, that was in the side of the yate biholdynge to the north; and the faces of tho weren ayens the south weie; oon of the side of the eest yate, that bihelde to the weie of the north.
45 Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
And he seide to me, This treserie, that biholdith the south weie, is of the prestis that waken in the kepyngis of the temple,
46 ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
Sotheli the tresorye that biholdith to the weie of the north, schal be of the preestis that waken to the seruice of the auter; these ben the sones of Sadoch, whiche of the sones of Leuy neiyen to the Lord, for to mynystre to hym.
47 Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
And he mat the halle, the lengthe of an hundrid cubitis, and the breede of an hundrid cubitis, bi square, and the auter bifore the face of the temple.
48 Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
And he ledde me in to the porche of the temple; and he mat the porche bi fyue cubitis on this side, and bi fyue cubitis on that side; and he mat the breede of the yate, of thre cubitis on this side, and of thre cubitis on that side.
49 Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.
But he mat the lengthe of the porche of twenti cubitis, and the breede of eleuene cubitis, and bi eiyte degrees me stiede to it; and pileris weren in the frountis, oon on this side, and `another on that side.

< Ezekieli 40 >