< Ezekieli 39 >

1 “Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
But profesie thou, sone of man, ayens Gog; and thou schalt seie, The Lord God seith these thingis, Lo! Y on thee, thou Gog, prince of the heed of Mosoch and of Tubal.
2 Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
And Y schal lede thee aboute, and Y schal disseyue thee, and Y schal make thee to stie fro the sidis of the north, and Y schal brynge thee on the hillis of Israel.
3 Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
And Y schal smyte thi bouwe in thi left hond, and Y schal caste doun thin arowis fro thi riyt hond.
4 Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
Thou schalt falle doun on the hillis of Israel, thou, and alle thi cumpenyes, and puplis that ben with thee; Y yaf thee for to be deuourid to wielde beestis, to briddis, and to ech volatil, and to the beestis of erthe.
5 Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Thou schalt falle doun on the face of the feeld; for Y the Lord haue spoke, seith the Lord God.
6 Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
And Y schal sende fier in Magog, and in hem that dwellen tristili in ilis; and thei schulen wite, that Y am the Lord God of Israel.
7 “Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
And Y schal make myn hooli name knowun in the myddis of my puple Israel, and Y schal no more defoule myn hooli name; and hethene men schulen wite, that Y am the Lord God, the hooli of Israel.
8 Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
Lo! it cometh, and it is don, seith the Lord God.
9 “Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
This is the day of which Y spak. And dwelleris schulen go out of the citees of Israel, and thei schulen set a fier, and schulen brenne armuris, scheeld and spere, bouwe and arowis, and stauys of hond, and schaftis with out irun; and thei schulen brenne tho in fier bi seuene yeer.
10 Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And thei schulen not bere trees of cuntries, nether schulen kitte doun of forestis, for thei schulen brenne armuris bi fier; and thei schulen take preies of hem, to whiche thei weren preies, and thei schulen rauysche her wasteris, seith the Lord God.
11 “Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
And it schal be in that dai, Y schal yyue to Gog a named place, a sepulcre in Israel, the valei of weigoeris at the eest of the see, that schal make hem that passen forth for to wondre; and thei schulen birie there Gog, and al the multitude of hym, and it schal be clepid the valei of the multitude of Gog.
12 “Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
And the hous of Israel schulen birie hem, that thei clense the lond in seuene monethis.
13 Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Forsothe al the puple of the lond schal byrie hym, and it schal be a named dai to hem, in which Y am glorified, seith the Lord God.
14 “Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
And thei schulen ordeyne bisili men cumpassynge the lond, that schulen birie and seke hem that weren left on the face of the lond, that thei clense it. Forsothe aftir seuene monethis thei schulen bigynne to seke,
15 Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
and thei schulen cumpas goynge aboute the lond; and whanne thei schulen se the boon of a man, thei schulen sette a `notable signe bisidis it, til the birieris of careyns birie it in the valei of the multitude of Gog.
16 (Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
Sotheli the name of the cite is Amona; and thei schulen clense the lond.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
Forsothe, thou, sone of man, the Lord God seith these thingis, Seie thou to ech brid, and to alle foulis, and to alle beestis of the feeld, Come ye to gidere, and haste ye, renne ye togidere on ech side to my sacrifice, which Y sle to you, a greet sacrifice on the hillis of Israel, that ye ete fleischis and drynke blood.
18 Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
Ye schulen ete the fleischis of stronge men, and ye schulen drynke the blood of prynces of erthe, of wetheris, of lambren, and of buckis of geet, and of bolis, and of beestis maad fat, and of alle fat thingis.
19 Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
And ye schulen ete the ynnere fatnesse in to fulnesse, and ye schulen drynke the blood in to drunkenesse, of the sacrifice which Y schal sle to you.
20 Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And ye schulen be fillid on my boord, of hors, and of strong horse man, and of alle men werriours, seith the Lord God.
21 “Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
And Y schal sette my glorie among hethene men, and alle hethene men schulen se my doom, which Y haue do, and myn hond, which Y haue set on hem.
22 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
And the hous of Israel schulen wite, that Y am her Lord God, fro that dai and afterward.
23 Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
And hethen men schulen wite, that the hous of Israel is takun in her wickidnesse, for that that thei forsoken me; and Y hidde my face fro hem, and Y bitook hem into the hondis of enemyes, and alle thei fellen doun bi swerd.
24 Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
Bi the unclennes and greet trespasse of hem Y dide to hem, and Y hidde my face fro hem.
25 “Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
Therfor the Lord God seith these thingis, Now Y schal leede ayen the caitiftee of Jacob, and Y schal haue merci on al the hous of Israel; and Y schal take feruoure for myn hooli name.
26 Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
And thei schulen bere here schenschipe, and al the trespassing bi which thei trespassiden ayens me, whanne thei dwelliden in her lond tristili, and dredden no man;
27 Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
and whanne Y schal bringe hem ayen fro puplis, and schal gadere fro the londis of her enemyes, and schal be halewid in hem, bifor the iyen of ful many folkis.
28 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
And thei schulen wite, that Y am the Lord God of hem, for that Y translatide hem in to naciouns, and haue gaderid hem on her lond, and Y lefte not ony of hem there.
29 Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
And Y schal no more hide my face fro hem, for Y haue schede out my spirit on al the hous of Israel, seith the Lord God.

< Ezekieli 39 >