< Ezekieli 11 >

1 Pamenepo Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kubwera nane ku chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Kumeneko pa khomo la chipata panali anthu 25, ndipo ndinaona pakati pawo atsogoleri awa: Yaazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya.
And the spirit reiside me, and ledde me with ynne to the eest yate of the hous of the Lord, that biholdith the risyng of the sunne. And lo! in the entryng of the yate weren fyue and twenti men; and Y siy in the myddis of hem Jeconye, the sone of Assur, and Pheltie, the sone of Banaie, princes of the puple.
2 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi anthu amene akukonza zoyipa ndi kupereka malangizo oyipa mu mzindamo.
And he seide to me, Thou, sone of man, these ben the men that thenken wickidnesse, and treten the worste counsel in this citee,
3 Iwo amawuza anthu kuti, ‘Nthawi sinafike yoti timange Nyumba? Mzindawu uli ngati mʼphika umene uli pa moto ndipo ife tili ngati nyama mu mʼphikamo.
and seien, Whether housis weren not bildid a while ago? this is the cawdrun, forsothe we ben fleischis.
4 Choncho iwe mwana wa munthu, unenere mowadzudzula. Nenera ndithu.’”
Therfor profesie thou of hem, profesie thou, sone of man.
5 Ndipo Mzimu wa Yehova unandigwera ndipo unandiwuza kuti, “Unene kuti zimene akunena Yehova ndi izi. Iye akuti. ‘Izi ndi zimene mukunena, Inu Aisraeli, koma Ine ndikudziwa zimene zili mu mtima mwanu.’
And the Spirit of the Lord felle in to me, and seide to me, Speke thou, The Lord seith these thingis, Ye hous of Israel spaken thus, and Y knewe the thouytis of youre herte;
6 Mwapha anthu ambiri mu mzinda muno ndipo mwadzaza misewu yake ndi mitembo.
ye killiden ful many men in this citee, and ye filliden the weies therof with slayn men.
7 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mitembo imene mwayiponya mʼmisewuyo ndiyo nyama ndipo mzinda uno ndiwo mʼphika, koma Ine ndidzakuthamangitsanimo.
Therfor the Lord seith these thingis, Youre slayn men, whiche ye puttiden in the myddis therof, these ben fleischis, and this is the cawdrun; and Y schal lede you out of the myddis therof.
8 Inu mumaopa lupanga, koma lupangalo ndi limene ndidzakubweretsereni, akutero Ambuye.
Ye dredden swerd, and Y schal brynge in swerd on you, seith the Lord God.
9 Ine ndidzakuthamangitsani mu mzinda ndipo ndidzakuperekani mʼdzanja la alendo kuti akulangeni.
And Y schal caste you out of the myddis therof, and Y schal yyue you in to the hond of enemyes, and Y schal make domes in you.
10 Mudzaphedwa ndi lupanga ndipo ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Bi swerd ye schulen falle doun, Y schal deme you in the endis of Israel; and ye schulen wite, that Y am the Lord.
11 Mzinda uno sudzakhala ngati mʼphika wokutetezani ndipo simudzakhalanso ngati nyama ya mʼmenemo. Ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli.
This schal not be to you in to a cawdrun, and ye schulen not be in to fleischis in the myddis therof; Y schal deme you in the endis of Israel,
12 Ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. Inu simunatsatire malangizo anga kapena kusunga malamulo anga koma mwakhala mukutsata zochita za mitundu ina ya anthu imene yakuzungulirani.’”
and ye schulen wite, that Y am the Lord. For ye yeden not in myn heestis, and ye dyden not my domes, but ye wrouyten bi the domes of hethene men, that ben in youre cumpas.
13 Tsono pamene ndinkanenera, Pelatiya mwana wa Benaya anafa. Pomwepo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba ndipo ndinafuwula ndi mawu aakulu kuti “Mayo, Ambuye Yehova! Kodi mudzawatheratu Aisraeli onse otsala?”
And it was doon, whanne Y profesiede, Pheltie, the sone of Banaie, was deed; and Y felle doun on my face, and Y criede with greet vois, and seide, Alas! alas! alas! Lord God, thou makist endyng of the remenauntis of Israel.
14 Yehova anayankhula nane kuti,
And the word of the Lord was maad to me,
15 “Anthu okhala ku Yerusalemu akuwanena abale ako, anthu a ku ukapolo, onse a banja la Israeli, kuti, ‘Anthu onse amene anatengedwa ukapolo ali kutali ndi Yehova. Dziko lanu Yehova anatipatsa kuti likhale lathulathu.’”
and he seide, Sone of man, thi britheren, thi kynes men, and al the hous of Israel, and alle men, to whiche the dwelleris of Jerusalem seiden, Go ye awei fer fro the Lord, the lond is youun to vs in to possessioun.
16 “Nʼchifukwa chake nena kwa anzako a ku ukapolo kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Ine ndinawatumiza kutali pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinawabalalitsa ku mayiko ambiri. Komabe ndakhala ndikuwasunga ku mayiko kumene anapitako!’
Therfor the Lord God seith these thingis, For Y made hem fer among hethene men, and for Y scateride hem in londis, Y schal be to hem in to a litil halewyng, in the londis to whiche thei camen.
17 “Nʼchifukwa chake uwawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kuti, Ndidzawasonkhanitsa kuchokera kwa anthu a mitundu inayo ndi kuwasonkhanitsira pamodzi kuchokera ku mayiko kumene ndinawabalalitsirako. Pambuyo pake ndidzawapatsa dziko la Israeli.
Therfor speke thou, The Lord God seith these thingis, Y schal gadere you fro puplis, and Y schal gadere you togidere fro londis, in whiche ye ben scatered; and Y schal yyue the erthe of Israel to you.
18 “Akadzalowa mʼdzikomo adzachotsa mafano awo onse oyipa ndi onyansa.
And thei schulen entre thidur, and schulen do awei alle offenciouns, and alle abhomynaciouns therof in that dai.
19 Ndidzawapatsa mtima watsopano ndipo ndidzayika mzimu watsopano mwa iwo. Ndidzachotsa mtima wowuma ngati mwala mwa iwo, ndipo ndidzawapatsa mtima wofewa ngati mnofu.
And Y schal yyue to hem oon herte, and Y schal yyue a newe spirit in the entrails of hem; and Y schal take awei a stony herte fro the fleisch of hem, and Y schal yyue to hem an herte of fleisch;
20 Motero adzatsata malamulo anga ndipo adzasunga mosamala malamulo anga. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
that thei go in my comaundementis, and kepe my domes, and do tho; and that thei be in to a puple to me, and Y be in to God to hem.
21 Koma kunena za amene akupembedza mafano oyipa ndi onyansa, ndidzawalanga chifukwa cha zimene achita. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
But of whiche the herte goith after her offendyngis and abhomynaciouns, Y schal sette the weie of hem in her heed, seith the Lord God.
22 Tsono akerubi aja anatambasula mapiko awo kuyamba kuwuluka, mikombero ili mʼmbali mwawo. Ulemerero wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
And the cherubyns reisiden her wyngis, and the wheelis yeden with tho, and the glorie of God of Israel was on tho.
23 Ulemerero wa Yehova unakwera ndi kusiya mzindawo ndipo unakayima pa phiri cha kummawa kwake kwa mzindawo.
And the glorie of the Lord stiede fro the myddis of the citee, and stood on the hil, which is at the eest of the citee.
24 Pambuyo pake Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kukandifikitsa. Zimenezi zinkachitika mʼmasomphenya monga mmene Mzimu wa Mulungu unkandionetsera. Kenaka masomphenya amene ndinkawaonawo anayamba kuzimirira.
And the spirit reiside me, and brouyte me in to Caldee, to the passyng ouer, in visioun bi the spirit of God; and the visioun which Y hadde seyn, was takun awei fro me.
25 Ndipo ndinafotokozera akapolowo zonse zimene Yehova anandionetsa.
And Y spak to the passyng ouer alle the wordis of the Lord, whiche he hadde schewid to me.

< Ezekieli 11 >