< Deuteronomo 7 >

1 Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
Kad te Gospod Bog tvoj uvede u zemlju u koju ideš da je naslijediš, i otjera ispred tebe narode mnoge, Heteje i Gergeseje i Amoreje i Hananeje i Ferezeje i Jeveje i Jevuseje, sedam naroda veæih i jaèih od tebe,
2 Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
I preda ih Gospod Bog tvoj tebi, i ti ih razbiješ, potri ih, ne hvataj s njima vjere, niti se smiluj na njih;
3 Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
Niti se prijatelji s njima; kæeri svoje ne daji za sina njihova, niti kæeri njihove uzimaj za sina svojega.
4 Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
Jer bi otpadila sina tvojega od mene, i služio bi bogovima drugim, te bi se razgnjevio Gospod na vas i potro vas brzo.
5 Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
Nego ovo im uèinite: oltare njihove raskopajte, i likove njihove polomite, lugove njihove isijecite, i rezane bogove njihove ognjem spalite.
6 Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
Jer si ti narod svet Gospodu Bogu svojemu, tebe je izabrao Gospod Bog tvoj da mu budeš narod osobit mimo sve narode na zemlji.
7 Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
Ne zato što bi vas bilo više nego drugih naroda prihvati vas Gospod i izabra vas; jer vas bijaše manje nego ikojega drugoga naroda;
8 Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
Nego što vas Gospod miluje i što drži zakletvu kojom se zakleo ocima vašim, zato vas je Gospod izveo rukom krjepkom i izbavio vas iz kuæe ropske, iz ruke Faraona cara Misirskoga.
9 Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
I tako znaj da je Gospod Bog tvoj Bog, Bog vjeran, koji drži zavjet svoj i milost svoju do tisuæu koljena onima koji ga ljube i drže zapovijesti njegove,
10 Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
I plaæa onima koji mrze na nj, svakome istrebljujuæi ga, i ne odgaða onome koji mrzi na nj, plaæa svakome.
11 Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
Zato drži zapovjesti i uredbe i zakone, koje ti danas ja zapovijedam, da ih tvoriš.
12 Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
I ako ove zakone uzaslušate i uzdržite i ustvorite, i Gospod æe Bog tvoj držati tebi zavjet i milost, za koju se zakleo ocima tvojim;
13 Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
I milovaæe te i blagosloviæe te i umnožiæe te; blagosloviæe plod utrobe tvoje i plod zemlje tvoje, žito tvoje i vino tvoje i ulje tvoje, plod goveda tvojih i stada ovaca tvojih u zemlji za koju se zakleo ocima tvojim da æe ti je dati.
14 Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
Biæeš blagosloven mimo sve narode: neæe biti u tebe ni muškoga ni ženskoga neplodna, ni meðu stokom tvojom.
15 Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
I ukloniæe od tebe Gospod svaku bolest, i od ljutih zala Misirskih koja znaš neæe nijednoga pustiti na tebe, nego æe ih pustiti na one sve koji mrze na te.
16 Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
I istrijebi sve narode koje ti Gospod Bog tvoj preda, neka ih ne požali oko tvoje, i nemoj služiti bogovima njihovijem, jer bi ti to bilo zamka.
17 Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
Ako bi rekao u srcu svom: veæi su ovi narodi od mene, kako ih mogu izagnati?
18 Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
Ne boj ih se; pamti dobro što je uèinio Gospod Bog tvoj s Faraonom i sa svijem Misircima,
19 Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
Velika kušanja, koja vidješe oèi tvoje, i znake i èudesa i ruku krjepku i mišicu podignutu, kojom te izvede Gospod Bog tvoj; onako æe uèiniti Gospod Bog tvoj sa svijem narodima od kojih bi se uplašio.
20 Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
I stršljene æe poslati Gospod Bog tvoj na njih dokle ne izginu koji bi ostali i sakrili se od tebe.
21 Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
Ne plaši se od njih, jer je Gospod Bog tvoj usred tebe, Bog veliki i strašni.
22 Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
Gospod æe Bog tvoj malo pomalo potrti te narode ispred tebe; neæeš ih moæi odjedanput istrijebiti, da se ne bi umnožilo na tebe zvijerje poljsko.
23 Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
Ali æe ih predati Gospod Bog tvoj tebi, i zatiraæe ih zatiranjem velikim dokle se ne zatru.
24 Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
I predaæe careve njihove u tvoje ruke da zatreš ime njihovo pod nebom, neæe se nijedan održati pred tobom, dokle ih ne potreš.
25 Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
Rezane bogove njihove spali ognjem, nemoj da se polakomiš na srebro ili zlato što je na njima i da ga uzmeš, da ti ne bude zamka, jer je gadno pred Gospodom Bogom tvojim.
26 Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.
I nemoj da uneseš gada u dom svoj, da ne budeš proklet kao i on, nego se gadi na nj i grozi se od njega, jer je prokleto.

< Deuteronomo 7 >