< Deuteronomo 6 >

1 Awa ndi malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene Yehova Mulungu wanu anandilamula kuti ndikuphunzitseni kuti mukawatsatire mʼdziko limene mukuwolokera Yorodani kuti mukalitenge,
A ovo su zapovijesti i uredbe i zakoni, koje Gospod Bog vaš zapovjedi da vas uèim da ih tvorite u zemlji u koju idete da je naslijedite,
2 kuti inuyo, ana anu, ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo mudzaope Yehova Mulungu wanu moyo wanu wonse posunga malangizo ndi malamulo ake onse amene ndinakupatsani inu kuti musangalale ndi moyo wautali.
Da bi se bojao Gospoda Boga svojega držeæi sve uredbe njegove i zapovijesti njegove, koje ti ja zapovijedam, ti i sin tvoj i unuk tvoj svega vijeka svojega, da bi ti se produljili dani tvoji.
3 Mvera Israeli ndipo usamalitse kuchita malamulowa kuti zinthu zikuyendere bwino mʼdziko ndi kuti muchuluke kwambiri mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
Èuj dakle, Izrailju, i gledaj da tako èiniš, da bi ti dobro bilo i da biste se umnožili veoma u zemlji u kojoj teèe mlijeko i med, kao što ti je rekao Gospod Bog otaca tvojih.
4 Tamvani inu Aisraeli, Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi.
Èuj, Izrailju: Gospod je Bog naš jedini Gospod.
5 Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse.
Zato ljubi Gospoda Boga svojega iz svega srca svojega i iz sve duše svoje i iz sve snage svoje.
6 Malamulo amene ndakupatsani lero ayenera kukhala mu mtima mwanu.
I neka ove rijeèi koje ti ja zapovijedam danas budu u srcu tvom.
7 Muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu. Muzikamba za malamulowa pamene muli mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mukugona ndi pamene mukudzuka.
I èesto ih napominji sinovima svojim, i govori o njima kad sjediš u kuæi svojoj i kad ideš putem, kad liježeš i kad ustaješ.
8 Muwamange ngati zizindikiro pa manja anu ndi kuwamangirira pa zipumi zanu.
I veži ih sebi na ruku za znak, i neka ti budu kao poèeonik meðu oèima.
9 Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu.
I napiši ih na dovratnicima od kuæe svoje i na vratima svojim.
10 Pamene Yehova Mulungu wanu akukulowetsani ndi kukupatsani dziko limene analumbirira makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo, dziko lokhala ndi mizinda ikuluikulu imene inu simunamange,
A kad te uvede Gospod Bog tvoj u zemlju za koju se zakleo ocima tvojim, Avramu, Isaku i Jakovu, da æe ti je dati, u gradove velike i dobre, kojih nijesi zidao,
11 nyumba zodzaza ndi zinthu za mitundu yonse zimene inu simunayikemo, zitsime zimene inu simunakumbe, minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi zimene inuyo simunadzale, tsono mukadya ndi kukhuta,
I kuæe pune svakoga dobra, kojih nijesi punio, i na studence iskopane, kojih nijesi kopao, u vinograde i u maslinike, kojih nijesi sadio, i staneš jesti i nasitiš se,
12 samalani kuti mungayiwale Yehova amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani mu ukapolo.
Èuvaj se da ne zaboraviš Gospoda, koji te je izveo iz zemlje Misirske, iz kuæe ropske.
13 Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye yekha, ndipo muzilumbira pa dzina lake.
Gospoda Boga svojega boj se, i njemu služi, i njegovim se imenom kuni.
14 Musamatsatire milungu ina, milungu ya anthu ena okuzungulirani,
Ne idite za drugim bogovima izmeðu bogova drugih naroda, koji su oko vas.
15 pakuti Yehova Mulungu wanu amene ali pakati panu, ndi Mulungu wansanje ndipo adzakukwiyirani kwambiri ndi kukuwonongani, kukufafanizani mʼdziko.
Jer je Bog revnitelj, Gospod Bog tvoj, usred tebe, pa da se ne bi razgnjevio Gospod Bog tvoj na te i istrijebio te sa zemlje.
16 Musamuyese Yehova Mulungu wanu monga munachitira ku Masa.
Nemojte kušati Gospoda Boga svojega kao što ga kušaste u Masi.
17 Onetsetsani kuti mukusunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, malangizo ake ndi zikhazikitso zake zimene anakulamulirani.
Držite dobro zapovijesti Gospoda Boga svojega i svjedoèanstva njegova i uredbe njegove, koje ti je zapovjedio,
18 Chitani zoyenera ndi zabwino pamaso pa Yehova, kuti zikuyendereni bwino ndi kuti mukhoza kukalowa ndi kulanda dziko labwinolo limene Yehova analonjeza molumbira kwa makolo anu,
I èini što je pravo i dobro pred Gospodom, da bi ti bilo dobro i da bi ušao u dobru zemlju, za koju se zakleo Gospod ocima tvojim, i da bi je naslijedio,
19 kupirikitsiratu adani anu onse, monga Yehova wanenera.
Da bi otjerao sve neprijatelje tvoje ispred tebe, kao što ti je rekao Gospod.
20 Mʼtsogolo muno, ana anu akadzakufunsani kuti, “Kodi tanthauzo la ndondomeko, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo amene Yehova Mulungu wathu anakulamulani nʼchiyani?”
Pa kad te zapita poslije sin tvoj govoreæi: kakva su to svjedoèanstva i uredbe i zakoni, što vam je zapovjedio Gospod Bog naš?
21 Inu mudzawawuze kuti, “Ife tinali akapolo a Farao ku Igupto, koma Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lamphamvu.
Onda kaži sinu svojemu: bijasmo robovi Faraonovi u Misiru, i izvede nas Gospod iz Misira rukom krjepkom,
22 Ifeyo tikuona Yehova anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, zazikulu ndi zoopsa, pa Aigupto ndi Farao pamodzi ndi banja lake lonse.
I uèini Gospod znake i èudesa velika i zla u Misiru na Faraonu i na svemu domu njegovu pred nama,
23 Koma anatitulutsa kumeneko ndi kutilowetsa kuno natipatsa dziko limene analonjeza mwa lumbiro kwa makolo athu.
A nas izvede odande da nas uvede u zemlju za koju se zakleo ocima našim da æe nam je dati.
24 Yehova anatilamula kuti tizimvera malamulo onsewa, kuti tizimuopa kuti zinthu zizitiyendera bwino pa moyo wathu monga momwe zilili leromu.
I zapovjedi nam Gospod da vršimo sve ove uredbe bojeæi se Gospoda Boga svojega, da bi nam bilo dobro svagda i da bi nas saèuvao u životu, kao što se vidi danas.
25 Ndipo ngati tisamala kumvera malamulo onsewa pamaso pa Yehova Mulungu wathu monga momwe anatilamulira ife, chimenecho chidzakhala chilungamo chathu.”
I biæe nam pravda, ako uzdržimo i ustvorimo sve zapovijesti ove pred Gospodom Bogom svojim, kako nam je zapovjedio.

< Deuteronomo 6 >