< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
A po smrti Mojsija sluge Gospodnjega reèe Gospod Isusu sinu Navinu, sluzi Mojsijevu, govoreæi:
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
Mojsije sluga moj umrije; zato sada ustani, prijeði preko toga Jordana ti i sav taj narod u zemlju koju ja dajem sinovima Izrailjevijem.
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
Svako mjesto na koje stupite stopama svojim dao sam vam, kao što rekoh Mojsiju.
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
Od pustinje i od ovoga Livana do rijeke velike, rijeke Efrata, sva zemlja Hetejska do velikoga mora na zapadu, biæe meða vaša.
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
Niko se neæe održati pred tobom svega vijeka tvojega; s tobom æu biti kao što sam bio s Mojsijem, neæu otstupiti od tebe niti æu te ostaviti.
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
Budi slobodan i hrabar, jer æeš ti predati tome narodu u našljedstvo zemlju za koju sam se zakleo ocima njihovijem da æu im je dati.
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
Samo budi slobodan i hrabar da držiš i tvoriš sve po zakonu koji ti je zapovjedio Mojsije sluga moj, ne otstupaj od njega ni nadesno ni nalijevo, da bi napredovao kuda god poðeš.
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
Neka se ne rastavlja od usta tvojih knjiga ovoga zakona, nego razmišljaj o njemu dan i noæ, da držiš i tvoriš sve kako je u njemu napisano; jer æeš tada biti sreæan na putovima svojim i tada æeš napredovati.
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
Nijesam li ti zapovjedio: budi slobodan i hrabar? ne boj se i ne plaši se; jer je s tobom Gospod Bog tvoj kuda god ideš.
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
Tada zapovjedi Isus upraviteljima narodnijem govoreæi:
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
Proðite kroz oko i zapovjedite narodu govoreæi: spremite sebi brašnjenice; jer æete do tri dana prijeæi preko Jordana da uðete i uzmete zemlju koju vam Gospod Bog vaš daje u našljedstvo.
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
A plemenu Ruvimovu i Gadovu i polovini plemena Manasijina reèe Isus govoreæi:
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
Opomenite se šta vam je zapovjedio Mojsije sluga Gospodnji rekav: Gospod Bog vaš smiri vas i dade vam ovu zemlju.
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
Žene vaše, djeca vaša i stoka vaša neka ostanu u zemlji koju vam dade Mojsije s ovu stranu Jordana; vi pak prijeðite pod oružjem pred braæom svojom, koji ste god za vojsku, i pomozite im,
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
Dokle ne smiri Gospod i braæu vašu kao vas, i naslijede i oni zemlju koju im daje Gospod Bog vaš; pa se onda vratite na našljedstvo svoje, koje vam je dao Mojsije sluga Gospodnji s ovu stranu Jordana k istoku, i držite ga.
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
A oni odgovoriše Isusu govoreæi: što si nam god zapovjedio èiniæemo, i kuda nas god pošlješ iæi æemo.
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
Slušaæemo te kako smo slušali Mojsija; samo neka Gospod Bog tvoj bude s tobom kao što je bio s Mojsijem.
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Ko bi se protivio tvojoj zapovijesti i ne bi slušao rijeèi tvojih u svemu što mu zapovjediš, neka se pogubi; samo budi slobodan i hrabar.

< Yoswa 1 >