< Deuteronomo 31 >

1 Tsono Mose anapita ndi kukayankhula mawu awa kwa Aisraeli onse:
Potom doðe Mojsije i kaza ove rijeèi svemu Izrailju,
2 “Tsopano ndili ndi zaka 120, ndipo sindingathenso kukutsogolerani. Yehova wandiwuza kuti, ‘Iwe sudzawoloka Yorodani.’
I reèe im: meni ima danas sto i dvadeset godina, ne mogu više odlaziti ni dolaziti; a i Gospod mi je rekao: neæeš prijeæi preko toga Jordana.
3 Mwini wake Yehova Mulungu wanu ndiye amene adzakutsogolerani powoloka. Iye adzawononga mitundu ina yonse, ndipo inu mudzatenga dziko lawo. Yoswa adzakutsogoleraninso powoloka, monga momwe ananenera Yehova.
Gospod æe Bog tvoj iæi pred tobom, i istrijebiæe one narode ispred tebe, i ti æeš ih naslijediti; Isus æe iæi pred tobom, kao što je kazao Gospod.
4 Ndipo Yehova adzawawononga iwo monga momwe anawonongera Sihoni ndi Ogi, mafumu Aamori, amene Iye anawawononga pamodzi ndi dziko lawo.
I uèiniæe Gospod s njima kako je uèinio sa Sionom i Ogom carevima Amorejskim i sa zemljom njihovom, te ih je istrijebio.
5 Ambuye adzawapereka kwa inu, ndipo inu mukawachitire zonse zimene ndakulamulani.
Zato kad vam ih preda Gospod uèinite im sasvijem onako kako sam vam zapovjedio.
6 Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
Budite slobodni i hrabri, i ne bojte se i ne plašite se od njih; jer Gospod Bog tvoj ide s tobom, neæe otstupiti od tebe, niti æe te ostaviti.
7 Pamenepo Yehova anayitana Yoswa pamaso pa Aisraeli onse ndipo anamuwuza kuti, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima, pakuti iwe udzatsogolera anthu awa ku dziko limene Yehova analumbira kulipereka kwa makolo awo, ndipo iwe ukaligawe pakati pawo kuti likakhale cholowa chawo.
Potom dozva Mojsije Isusa, i reèe mu pred svijem Izrailjem: budi slobodan i hrabar; jer æeš ti uæi s ovijem narodom u zemlju za koju se zakleo Gospod ocima njihovijem da æe im je dati, i ti æeš im je razdijeliti u našljedstvo.
8 Yehova mwini ndiye akukutsogolerani ndipo adzakhala nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani. Usachite mantha ndiponso usataye mtima.”
Jer Gospod koji ide pred tobom biæe s tobom, neæe otstupiti od tebe, niti æe te ostaviti, ne boj se i ne plaši se.
9 Choncho Mose analemba malamulo awa nawapereka kwa ansembe, ana Alevi, amene amanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, ndiponso kwa akuluakulu onse a Aisraeli.
I Mojsije napisa ovaj zakon, i dade ga sveštenicima, sinovima Levijevim, koji nošahu kovèeg zavjeta Gospodnjega, i svijem starješinama Izrailjevijem.
10 Kenaka Mose anawalamula kuti, “Pamapeto pa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, chaka cha kukhululukidwa ngongole, pa nthawi ya Chikondwerero cha Misasa,
I zapovjedi im Mojsije govoreæi: svake sedme godine, u odreðeno vrijeme godine oprosne, na praznik sjenica,
11 pamene Aisraeli onse abwera kudzaonekera pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamalo pamene Iye adzasankhe, mudzawerenge malamulo onsewa iwo akumva.
Kad doðe sav Izrailj i stane pred Gospoda Boga svojega na mjestu koje izbere, èitaj ovaj zakon pred svijem Izrailjem da èuju,
12 Mudzasonkhanitse anthu onse pamodzi, amuna, akazi ndi ana pamodzi ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu, kuti adzawamve ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamala mawu onse a mʼmalamulowa.
Sabravši narod, ljude i žene i djecu i došljake, koji budu u mjestima tvojim, da èuju i uèe i da se boje Gospoda Boga vašega, i drže i tvore sve rijeèi ovoga zakona;
13 Ana awo amene sadziwa malamulo awa, ayenera kuwamva ndi kuphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse pamene mukukhala mʼdziko limene mukuwoloka Yorodani kukalitenga.”
I sinovi njihovi, koji još ne znaju, neka èuju i uèe bojati se Gospoda Boga vašega, dokle ste god živi na zemlji u koju idete preko Jordana da je naslijedite.
14 Yehova anawuza Mose kuti, “Nthawi ya kufa kwako yafika. Itana Yoswa ndipo mubwere ku tenti ya msonkhano, kumene Ine ndidzamulangiza.” Choncho Mose ndi Yoswa anabwera ku tenti ya msonkhano.
A Gospod reèe Mojsiju: evo, približi se vrijeme da umreš. Dozovi Isusa i stanite obojica u šatoru od sastanka, da mu dam zapovijesti. I otide Mojsije i Isus, i stadoše u šatoru od sastanka.
15 Pamenepo Yehova anaonekera ku tenti mʼchipilala cha mtambo, ndipo mtambowo unayima pamwamba pa khomo lolowera mu tenti.
I javi se Gospod u šatoru u stupu od oblaka, i stajaše stup od oblaka nad vratima od šatora.
16 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, “Iwe ukupita kukapuma kumene kuli makolo ako, ndipo ukangomwalira, anthu awa adzayamba kupembedza milungu yachilendo ya mʼdziko limene akukalowamo. Adzanditaya ndi kuphwanya pangano lomwe ndinachita nawo.
I reèe Gospod Mojsiju: evo, ti æeš poèinuti s ocima svojim; a narod ovaj ustavši èiniæe preljubu za tuðim bogovima one zemlje u koju ide, i ostaviæe me i pokvariæe zavjet moj, koji uèinih s njima.
17 Tsiku limenelo Ine ndidzawakwiyira ndi kuwataya. Ndidzawabisira nkhope yanga, ndipo adzawonongedwa. Masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, ndipo tsiku limenelo adzafunsa kuti, ‘Kodi masautso awa sanagwere ife chifukwa Yehova Mulungu wathu sali nafe?’
I onda æe se raspaliti moj gnjev na njih, i ostaviæu ih, i sakriæu lice svoje od njih; oni æe se proždrijeti, i snaæi æe ih zla mnoga i nevolje; i onda æe reæi: da me ne snaðoše ova zla zato što Bog moj nije posred mene?
18 Ndipo Ine ndidzabisa ndithu nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoyipa zimene anachita potembenukira kwa milungu ina.
A ja æu onda sasvijem sakriti lice svoje za sva zla koja uèiniše obrativši se k drugim bogovima.
19 “Tsopano ulembe mawu a nyimbo iyi ndipo uwaphunzitse Aisraeli, uwawuze kuti aziyimba, kuti ikhale mboni yanga yowatsutsa.
Zato sad napišite sebi ovu pjesmu, i nauèi je sinove Izrailjeve; metni im je u usta da mi ta pjesma bude svjedok na sinove Izrailjeve.
20 Pamene ndawalowetsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, dziko limene ndinalonjeza mwalumbiro kwa makolo awo, ndipo pamene adzadya ndi kukhuta ndi kumasangalala, iwo adzatembenukira kwa milungu ina ndi kumayipembedza, kundikana Ine ndi kuphwanya pangano langa.
Jer æu ga odvesti u zemlju za koju sam se zakleo ocima njegovijem, u kojoj teèe mlijeko i med; ondje æe jesti i nasitiæe se i ugojiæe se, pa æe se onda obratiti k drugim bogovima i njima æe služiti, a za mene neæe mariti, i pokvariæe zavjet moj.
21 Ndipo pamene masautso ambiri ndi zovuta zambiri zidzawagwera, nyimbo iyi idzakhala mboni yanga yowatsutsa, chifukwa zidzukulu zawo sizidzayiwala nyimboyi. Ine ndikudziwa zimene iwo akulingalira kuchita, ngakhale kuti sindinawalowetse mʼdziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro.”
A kad ga snaðu zla mnoga i nevolje, onda æe ta pjesma svjedoèiti na njih; jer se neæe zaboraviti niti æe je nestati iz usta sjemena njihova. Jer znam misli njihove i što æe još danas èiniti, prije nego ih uvedem u zemlju za koju sam se zakleo.
22 Choncho Mose analemba nyimbo iyi tsiku limenelo ndi kuwaphunzitsa Aisraeli.
I napisa Mojsije tu pjesmu onaj dan, i nauèi sinove Izrailjeve.
23 Yehova analamula Yoswa mwana wa Nuni kuti, “Khala wamphamvu ndipo limba mtima, chifukwa udzalowetsa Aisraeli mʼdziko limene ndinawalonjeza mwa lumbiro, ndipo Ine mwini ndidzakhala nawe.”
I Gospod dade zapovijesti Isusu sinu Navinu govoreæi: budi slobodan i hrabar, jer æeš ti uvesti sinove Izrailjeve u zemlju za koju sam im se zakleo, i ja æu biti s tobom.
24 Mose atatha kulemba malamulowa mʼbuku, osasiyako kanthu,
I kad napisa Mojsije rijeèi ovoga zakona u knjigu, sve do kraja,
25 analamula Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova kuti,
Zapovjedi Mojsije Levitima, koji nošahu kovèeg zavjeta Gospodnjega, govoreæi:
26 “Tengani Buku ili la Malamulo ndi kuliyika pambali pa Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu. Likhale kumeneko ngati mboni yokutsutsani.
Uzmite ovu knjigu zakona, i metnite je pokraj kovèega zavjeta Gospoda Boga svojega, da bude ondje svjedok na vas.
27 Pakuti Ine ndikudziwa kuwukira kwanu ndi kuwuma mtima kwanu. Ngati inu mwakhala mukuwukira Yehova ine ndili moyo ndiponso ndili nanu pamodzi, nanga mudzawukira motani ine ndikamwalira!
Jer znam nepokornost tvoju i tvrdi vrat tvoj. Eto, dokle sam još živ s vama, do danas, bijaste nepokorni Gospodu; akamoli kad ja umrem?
28 Mundisonkhanitsire atsogoleri onse a mafuko anu pamodzi ndi akuluakulu onse, kuti ndiyankhule mawu awa iwo akumva ndipo kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni yowatsutsa.
Skupite k meni sve starješine od plemena svojih i upravitelje svoje da im kažem da èuju ove rijeèi, i da im zasvjedoèim nebom i zemljom.
29 Chifukwa ndikudziwa kuti ine ndikamwalira mudzayipa kwambiri ndi kutembenuka kuleka njira imene ndinakulamulani. Masiku amene akubwera, masautso adzakugwerani chifukwa mudzachita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuputa mkwiyo wake chifukwa cha zimene manja anu anapanga.”
Jer znam da æete se po smrti mojoj pokvariti, i zaæi s puta koji vam zapovjedih; i zato æe vas zadesiti ovo zlo najposlije, kad stanete èiniti što je zlo pred Gospodom gnjeveæi ga djelom ruku svojih.
30 Ndipo Mose ananena mawu a nyimbo iyi kuyiimba koyambira mpaka potsiriza gulu lonse la Aisraeli likumva:
I izgovori Mojsije da èuje sav zbor Izrailjev rijeèi ove pjesme do kraja:

< Deuteronomo 31 >