< Deuteronomo 30 >

1 Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu,
A kad doðe na tebe sve ovo, blagoslov i kletva koju iznesoh preda te, ako ih se opomeneš u srcu svom, gdje bi god bio meðu narodima, u koje te zagna Gospod Bog tvoj,
2 ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino,
I obratiš se ka Gospodu Bogu svojemu i poslušaš glas njegov u svemu što ti ja zapovijedam danas, ti i sinovi tvoji, iz svega srca svojega i iz sve duše svoje,
3 pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani.
Tada æe Gospod Bog tvoj povratiti roblje tvoje i smilovaæe se na tebe, i opet æe te sabrati izmeðu svijeh naroda, po kojima te bude rasijao Gospod Bog tvoj.
4 Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso.
Ako bi ko tvoj i na kraj svijeta zagnan bio, otuda æe te opet sabrati Gospod Bog tvoj i otuda te uzeti.
5 Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu.
I odvešæe te opet Gospod Bog tvoj u zemlju koju bijahu naslijedili oci tvoji, i naslijediæeš je, i uèiniæe ti dobro i umnožiæe te veæma nego oce tvoje.
6 Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo.
I obrezaæe Gospod Bog tvoj srce tvoje i srce sjemena tvojega, da bi ljubio Gospoda Boga svojega iz svega srca svojega i iz sve duše svoje, da budeš živ.
7 Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani.
A sve kletve ove obratiæe Gospod Bog tvoj na neprijatelje tvoje i na nenavidinike tvoje, koji su te gonili.
8 Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino.
A ti kad se obratiš i staneš slušati glas Gospoda Boga svojega i tvoriti sve zapovijesti njegove, koje ti ja danas zapovijedam,
9 Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu,
Daæe ti Gospod Bog tvoj sreæu u svakom djelu ruku tvojih, u plodu utrobe tvoje, u plodu stoke tvoje, u plodu zemlje tvoje; jer æe ti se Gospod Bog tvoj opet radovati èineæi ti dobro, kao što se radovao ocima tvojim,
10 ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
Ako uzaslušaš glas Gospoda Boga svojega držeæi sve zapovijesti njegove i uredbe njegove, napisane u knjizi ovoga zakona; kad se obratiš ka Gospodu Bogu svojemu svijem srcem svojim i svom dušom svojom.
11 Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali.
Jer zapovijest ova koju ti ja zapovijedam danas niti je visoko ni daleko od tebe;
12 Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
Nije na nebu, da reèeš: ko æe nam se popeti na nebo da nam je skine i kaže nam je, da bismo je tvorili?
13 Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
Niti je preko mora, da reèeš: ko æe nam otiæi preko mora, da nam je donese i kaže nam je, da bismo je tvorili?
14 Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.
Nego ti je vrlo blizu ova rijeè, u ustima tvojima i u srcu tvojem, da bi je tvorio.
15 Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko.
Gle, iznesoh danas preda te život i dobro, smrt i zlo.
16 Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.
Jer ti zapovijedam danas da ljubiš Gospoda Boga svojega hodeæi putovima njegovijem i držeæi zapovijesti njegove i uredbe njegove i zakone njegove, da bi živ bio i umnožio se, i da bi te blagoslovio Gospod Bog tvoj u zemlji u koju ideš da je naslijediš.
17 Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza,
Ako li se odvrati srce tvoje i ne uzaslušaš, nego zastraniš da se klanjaš drugim bogovima i njima služiš,
18 lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.
Javljam vam danas da æete zaista propasti, niti æete produljiti dana svojih na zemlji, u koju ideš preko Jordana da je naslijediš.
19 Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo.
Svjedoèim vam danas nebom i zemljom, da sam stavio pred vas život i smrt, blagoslov i prokletstvo; zato izberi život, da budeš živ ti i sjeme tvoje,
20 Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
Ljubeæi Gospoda Boga svojega, slušajuæi glas njegov i držeæi se njega; jer je on život tvoj i duljina dana tvojih; da bi nastavao na zemlji, za koju se zakleo Gospod ocima tvojim, Avramu, Isaku i Jakovu, da æe im je dati.

< Deuteronomo 30 >