< 2 Mbiri 36 >

1 Tsono anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namuyika kukhala mfumu mu Yerusalemu mʼmalo mwa abambo ake.
Tada uze narod zemaljski Joahaza sina Josijina, i zacariše ga na mjesto oca njegova u Jerusalimu.
2 Yowahazi anali wa zaka 23 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu.
Dvadeset i tri godine imaše Joahaz kad poèe carovati, i carova tri mjeseca u Jerusalimu.
3 Mfumu ya Igupto inamuchotsa pa udindo wa ufumu mu Yerusalemu ndipo inakhometsa msonkho dziko la Yuda wa makilogalamu 3,400 asiliva ndi agolide.
Jer ga svrže car Misirski u Jerusalimu i oglobi zemlju sto talanata srebra i talanat zlata.
4 Mfumu ya Igupto inakhazika Eliyakimu, mʼbale wake wa Yehowahazi kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu ndipo anasintha dzina la Eliyakimu kukhala Yehoyakimu. Koma Neko anatenga Yowahazi mʼbale wake wa Eliyakimu ndi kupita naye ku Igupto.
I postavi car Misirski Elijakima brata njegova carem nad Judom i Jerusalimom, i predje mu ime Joakim; a Joahaza brata njegova uze Nehaon i odvede ga u Misir.
5 Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake.
Dvadeset i pet godina bijaše Joakimu kad poèe carovati, i carova jedanaest godina u Jerusalimu; i èinjaše zlo pred Gospodom Bogom svojim.
6 Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anachita naye nkhondo ndipo anamumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kumutenga kupita naye ku Babuloni.
I doðe na nj Navuhodonosor car Vavilonski, i sveza ga u dvoje verige mjedene i odvede ga u Vavilon.
7 Nebukadinezara anatenganso zipangizo za ku Nyumba ya Yehova kupita nazo ku Babuloni ndipo anaziyika mʼnyumba ya Mulungu wake kumeneko.
I sudove doma Gospodnjega odnese Navuhodonosor u Vavilon, i metnu ih u crkvu svoju u Vavilonu.
8 Zochitika zina za pa ulamuliro wa Yehoyakimu, zinthu zonyansa zimene anachita ndi zonse zinapezeka kuti zinali zomutsutsa zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
A ostala djela Joakimova i gadovi koje je èinio, i što se na njemu naðe, eto, to je zapisano u knjizi o carevima Izrailjevijem i Judinijem; i zacari se na njegovo mjesto Joahin sin njegov.
9 Yehoyakini anali ndi zaka 21 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu ndi masiku khumi. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
Bijaše Joahinu osam godina kad poèe carovati, i carova tri mjeseca i deset dana u Jerusalimu; i èinjaše što je zlo pred Gospodom.
10 Nthawi ya mphukira, mfumu Nebukadinezara inayitanitsa Yehoyakini ndipo inapita naye ku Babuloni, pamodzi ndi ziwiya zamtengowapatali za mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova, ndipo anayika Zedekiya malume wake kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.
I kad proðe ona godina, posla car Navuhodonosor, te ga odnesoše u Vavilon sa zakladima doma Gospodnjega, a carem postavi Sedekiju brata njegova nad Judom i Jerusalimom.
11 Zedekiya anali ndi zaka 21 pamene ankakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11.
Dvadeset i jedna godina bijaše Sedekiji kad poèe carovati, i carova jedanaest godina u Jerusalimu.
12 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake ndipo sanadzichepetse yekha pamaso pa mneneri Yeremiya amene ankayankhula mawu a Yehova.
I èinjaše zlo pred Gospodom Bogom svojim, i ne pokori se pred Jeremijom prorokom, koji mu govoraše iz usta Gospodnjih;
13 Iye anawukiranso mfumu Nebukadinezara amene anamulumbiritsa mʼdzina la Mulungu. Iyeyo anali wosamva ndipo anawumitsa mtima wake. Sanatembenukire kwa Yehova Mulungu wa Israeli.
Nego se još odvrže od cara Navuhodonosora, koji ga bješe zakleo Bogom; i otvrdnu vratom svojim i uprije se srcem svojim da se ne obrati ka Gospodu Bogu Izrailjevu.
14 Kuwonjezera apo, atsogoleri onse a ansembe ndi anthu ena anapitirapitira kukhala osakhulupirika, kutsatira machitidwe onse onyansa a mitundu ina ndi kudetsa Nyumba ya Yehova Mulungu wawo, imene anayipatula mu Yerusalemu.
I svi glavari izmeðu sveštenika i narod griješiše veoma mnogo po svijem gadnijem djelima drugih naroda, skvrneæi dom Gospodnji, koji bješe osvetio u Jerusalimu.
15 Yehova, Mulungu wa makolo awo, ankatumiza mawu kwa iwo kudzera kwa amithenga ake kawirikawiri, chifukwa ankawamvera chisoni anthu ake ndi malo ake okhalapo.
I Gospod Bog otaca njihovijeh slaše k njima zarana jednako glasnike svoje, jer mu bješe žao naroda njegova i stana njegova.
16 Koma iwo ananyoza amithenga a Mulungu, anapeputsa mawu awo ndipo ankaseka aneneri ake mpaka anawutsa mkwiyo wa Yehova pa anthu ake ndipo panalibenso mankhwala owachiritsa.
A oni se rugahu glasnicima Božjim, i ne marahu za rijeèi njegove, i smijahu se prorocima njegovijem, dokle se ne raspali gnjev Gospodnji na narod njegov, te ne bi lijeka.
17 Yehova anabweretsa mfumu ya anthu a ku Babuloni, imene inapha anyamata awo ndi lupanga ku malo opatulika, ndipo sanasiye kaya mnyamata kapena mtsikana, wamkulu kapena wokalamba. Mulungu anapereka onsewo kwa Nebukadinezara.
I dovede na njih cara Haldejskoga, koji pobi mladiæe njihove maèem u domu svetinje njihove, i ne požali ni mladiæa ni djevojke, ni starca ni nemoæna. Sve mu dade u ruke.
18 Iye ananyamula kupita nazo ku Babuloni zipangizo zonse za mʼNyumba ya Yehova Mulungu wawo, zazikulu ndi zazingʼono zomwe, ndi chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso chuma cha mfumu ndi akuluakulu ake.
I sve sudove doma Božijega, velike i male, i blago doma Gospodnjega i blago carevo i knezova njegovijeh, sve odnese u Vavilon.
19 Iwo anayatsa moto Nyumba ya Mulungu, ndipo anagwetsa makoma a Yerusalemu. Anatentha moto nyumba zonse zaufumu ndipo anawononga chilichonse chimene chinali chofunika.
I upališe dom Božji, i razvališe zid Jerusalimski, i sve dvorove u njemu popališe ognjem, i iskvariše sve dragocjene zaklade njegove.
20 Iye anagwira ukapolo anthu otsala amene anapulumuka ku lupanga ndi kupita nawo ku Babuloni, ndipo anakhala antchito ake ndi ana ake mpaka pamene ufumu wa Peresiya unakhazikitsidwa.
I što ih osta od maèa, odnese ih u Vavilon i biše robovi njemu i sinovima njegovijem, dokle ne nasta carstvo Persijsko,
21 Dziko linakondwera ndi masabata ake. Pa nthawi yonse ya chipasuko chake nthaka inapuma, mpaka zaka 70 zinakwana pokwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya.
Da se ispuni rijeè Gospodnja koju reèe ustima Jeremijinijem, dokle se zemlja ne izdovolji subotama svojim, jer poèivaše za sve vrijeme dokle bješe pusta, dokle se ne navrši sedamdeset godina.
22 Mʼchaka choyamba cha Koresi mfumu ya Peresiya, pofuna kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anakhudza mtima wa mfumu ya Peresiya kuti alengeze mu ufumu wake wonse ndipo anazilemba:
Ali prve godine Kira cara Persijskoga, da bi se ispunila rijeè Gospodnja koju reèe na usta Jeremijina, podiže Gospod duh Kira cara Persijskoga, te oglasi po svemu carstvu svojemu i raspisa govoreæi:
23 Chimene mfumu Koresi ya Peresiya ikunena ndi ichi: “Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa ine mafumu onse a dziko lapansi ndipo wandisankha kuti ndimumangire Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ku Yuda. Aliyense wa anthu ake pakati panu, Yehova Mulungu wake akhale naye, ndipo apite.”
Ovako veli Kir car Persijski: sva carstva zemaljska dao mi je Gospod Bog nebeski, i on mi je zapovjedio da mu sazidam dom u Jerusalimu u Judeji. Ko je izmeðu vas od svega naroda njegova? Gospod Bog njegov neka bude s njim, pa nek ide.

< 2 Mbiri 36 >