< Ezara 1 >

1 Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi mfumu ya Perisiya, pofuna kukwaniritsa zimene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anayika maganizo mu mtima mwa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mʼdziko lake lonse ndi mawu apakamwa ngakhalenso ochita kulemba.
Prve godine Kira cara Persijskoga, da bi se ispunila rijeè Gospodnja, koju reèe na usta Jeremijina, podiže Gospod duh Kira cara Persijskoga, te oglasi po svemu carstvu svojemu i raspisa govoreæi:
2 Iye anati, “Koresi mfumu ya Perisiya ikunena kuti, “‘Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse a dziko lapansi, ndipo wandipatsa udindo woti ndimumangire Nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda.
Ovako veli Kir car Persijski: sva carstva zemaljska dao mi je Gospod Bog nebeski, i on mi je zapovjedio da mu sazidam dom u Jerusalimu u Judeji.
3 Aliyense wa inu amene ali wa Yehova, Mulungu wakeyo akhale naye. Tsono aliyense wa inu apite ku Yerusalemu, mʼdziko la Yuda kuti akamange Nyumba ya Yehova, Mulungu wa Israeli. Iyeyu ndi Mulungu amene ali mu Yerusalemu.
Ko je izmeðu vas od svega naroda njegova? Bog nebeski neka bude s njim, pa nek ide u Jerusalim u Judeji, i neka zida dom Gospoda Boga Izrailjeva, Boga koji je u Jerusalimu.
4 Ndipo kumalo kulikonse kumene otsalawo akukhala, athandizidwe ndi eni dzikolo powapatsa siliva, golide, katundu ndi ziweto ndi zopereka za ufulu zoti akapereke ku Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.’”
A ko bi ostao u kojem god mjestu gdje se bavi, neka ga ljudi onoga mjesta potpomognu srebrom i zlatom i imanjem i stokom osim dragovoljnoga priloga na dom Božji u Jerusalimu.
5 Choncho atsogoleri a mabanja afuko la Yuda ndi la Benjamini komanso ansembe ndi Alevi, aliyense amene Mulungu anawutsa mtima wake, anayamba kukonzeka kupita kukamanga Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.
Tada ustaše glavari porodica otaèkih od Jude i Venijamina, i sveštenici i Leviti i svi kojima Bog podiže duh da idu da zidaju dom Gospodnji u Jerusalimu.
6 Onse oyandikana nawo anawathandiza powapatsa ziwiya za siliva ndi zagolide, kuphatikizaponso katundu ndi ziweto, ndiponso mphatso zamtengo wapatali, kuwonjezera pa zopereka zaufulu zija.
I potpomogoše ih svi koji bijahu oko njih sudovima srebrnijem i zlatnijem, imanjem i stokom i stvarima skupocjenijem osim svega što dragovoljno priložiše.
7 Nayenso mfumu Koresi anatulutsa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara anazitenga kuzichotsa ku Yerusalemu ndi kuziyika mʼnyumba ya milungu yake.
I car Kir izdade sudove doma Gospodnjega koje bijaše odnio iz Jerusalima car Navuhodonosor i metnuo u dom svojih bogova;
8 Koresi, mfumu ya ku Perisiya inatulutsa ziwiyazi ndi kuzipereka kwa Miteridati, msungichuma amene anaziwerenga pamaso pa Sesibazara nduna yayikulu ya dziko la Yuda.
A izdade ih Kir car Persijski preko Mitridata riznièara, koji ih izbroji Sasavasaru knezu Judejskom.
9 Chiwerengerochi chinali motere: Mabeseni agolide 30 mabeseni asiliva 1,000 a zopereka 29
A ovo im je broj: zdjela zlatnijeh trideset, zdjela srebrnijeh tisuæa, noževa dvadeset i devet,
10 timiphika tagolide 230 timiphika tasiliva 410 ziwiya zina 1,000.
Èaša zlatnijeh trideset, drugih èaša srebrnijeh èetiri stotine i deset, drugih sudova tisuæa;
11 Ziwiya zonse zagolide ndi siliva pamodzi zinalipo 5,400. Zonsezi ndi zimene Sezi-Bazara anabwera nazo pamene otengedwa ukapolo aja ankabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku Babuloni.
Svega sudova zlatnijeh i srebrnijeh pet tisuæa i èetiri stotine; sve to ponese Sasavasar kad se vrati iz Vavilona u Jerusalim.

< Ezara 1 >