< 2 Mbiri 35 >

1 Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
I praznova Josija u Jerusalimu pashu Gospodu; i klaše pashu èetrnaestoga dana prvoga mjeseca.
2 Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
I postavi sveštenike u službe njihove, i utvrdi ih da služe u domu Gospodnjem.
3 Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
I reèe Levitima, koji uèahu vas narod Izrailjev i bijahu posveæeni Gospodu: namjestite sveti kovèeg u domu koji je sazidao Solomun sin Davidov car Izrailjev, ne treba više da ga nosite na ramenima; sada služite Gospodu Bogu svojemu i narodu njegovu Izrailju.
4 Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
I pripravite se po domovima otaca svojih po redovima svojim kako je naredio David car Izrailjev i Solomun sin njegov.
5 “Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
I stojte u svetinji po redovima domova otaèkih braæe svoje, sinova narodnijeh, i po redovima domova otaèkih meðu Levitima.
6 Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
I tako zakoljite pashu, i osveštajte se i pripravite braæu svoju da bi èinili kako je rekao Gospod preko Mojsija.
7 Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
I Josija dade narodu od stoke jaganjaca i jariæa, sve za pashu, svjema koji bijahu ondje, na broj dvije tisuæe i šest stotina, i tri tisuæe goveda, sve od careva blaga.
8 Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
I knezovi njegovi dadoše dragovoljno narodu, sveštenicima i Levitima: Helkija i Zaharija i Jehilo starješine u domu Božijem dadoše sveštenicima za pashu dvije tisuæe i šest stotina jaganjaca i jariæa i tri stotine goveda.
9 Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
A Honanija i Semaja i Natanailo braæa njegova, i Asavija i Jeilo i Jozavad, poglavari Levitski dadoše Levitima za pashu pet tisuæa jaganjaca i jariæa, i pet stotina goveda.
10 Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
I kad bi spremljeno za službu, stadoše sveštenici na svoje mjesto i Leviti u redovima svojim po zapovijesti carevoj.
11 Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
I klahu pashu, i sveštenici kropljahu krvlju primajuæi iz njihovijeh ruku, a Leviti derahu.
12 Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
I odvojiše žrtvu paljenicu da dadu narodu po redovima domova otaèkih da se prinese Gospodu, kako je napisano u knjizi Mojsijevoj. Tako uèiniše i s govedima.
13 Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
I pekoše pashu na ognju po obièaju; a druge posveæene stvari kuhaše u loncima i u kotlovima i u tavama, i razdavaše brzo svemu narodu.
14 Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
Potom gotoviše sebi i sveštenicima; jer sveštenici sinovi Aronovi imahu posla oko žrtava paljenica i pretilina do noæi; zato Leviti gotoviše i sebi i sveštenicima sinovima Aronovijem.
15 Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
I pjevaèi sinovi Asafovi stajahu na svom mjestu po zapovijesti Davidovoj i Asafovoj i Emanovoj i Jedutuna vidioca careva; i vratari na svakim vratima; ne micahu se od službe svoje, nego braæa njihova, ostali Leviti, gotoviše im.
16 Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
Tako bi ureðena sva služba Gospodnja u onaj dan da se proslavi pasha i prinesu žrtve paljenice na oltaru Gospodnjem po zapovijesti cara Josije.
17 Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
I praznovaše sinovi Izrailjevi koji se naðoše ondje pashu u to vrijeme i praznik prijesnijeh hljebova sedam dana.
18 Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
I ne bi pasha praznovana kao ova u Izrailju od vremena Samuila proroka, niti koji careva Izrailjevijeh praznova pashu kao što je praznova Josija sa sveštenicima i Levitima i sa svijem Judom i Izrailjem što ga se naðe, i s Jerusalimljanima.
19 Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
Osamnaeste godine carovanja Josijina praznovana bi ta pasha.
20 Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
Poslije svega toga, kad Josija uredi dom, doðe Nehaon car Misirski da bije Harkemis na Efratu, i Josija izide preda nj.
21 Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
A on posla k njemu poslanike i poruèi: šta ja imam s tobom, care Judin? ne idem ja danas na tebe, nego na dom koji vojuje na mene, i Bog mi je zapovjedio da pohitam. Proði se Boga koji je sa mnom, da te ne ubije.
22 Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
Ali se Josija ne odvrati od njega, nego se preobuèe da se bije s njim, i ne posluša rijeèi Nehaonovijeh iz usta Božjih, nego doðe da se pobije u polju Megidonskom.
23 Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
I strijelci ustrijeliše cara Josiju, i car reèe slugama svojim: izvezite me odavde, jer sam ljuto ranjen.
24 Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
I skidoše ga sluge njegove s kola, i metnuše na druga kola koja imaše, i odvezoše ga u Jerusalim; i umrije, i bi pogreben u groblju otaca svojih. I sav Juda i Jerusalim plaka za Josijom.
25 Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
I prorok Jeremija narica za Josijom. I svi pjevaèi i pjevaèice spominjaše u tužbalicama svojim Josiju do današnjega dana, i uvedoše ih u obièaj u Izrailju, i eto napisane su u plaèu.
26 Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
A ostala djela Josijina i milostinje njegove, kako piše u zakonu Gospodnjem,
27 zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
Djela njegova prva i pošljednja, eto zapisana su u knjizi o carevima Izrailjevijem i Judinijem.

< 2 Mbiri 35 >