< 2 Mbiri 28 >

1 Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
Dvadeset godina bijaše Ahazu kad poèe carovati, i carova šesnaest godina u Jerusalimu; ali ne èinjaše što je pravo pred Gospodom kao David otac njegov.
2 Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
Jer hoðaše putovima careva Izrailjevijeh, i još sali likove Valima.
3 Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
I sam kaðaše u dolini sina Enomova, i sažizaše sinove svoje ognjem po gadnijem djelima onijeh naroda koje odagna Gospod ispred sinova Izrailjevijeh.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
I prinošaše žrtve i kaðaše na visinama i po brdima i pod svakim zelenijem drvetom.
5 Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
Zato ga dade Gospod Bog njegov u ruke caru Sirskomu, te ga razbiše i zarobiše mu veliko mnoštvo, i odvedoše ih u Damasak. Još bi dat u ruke i caru Izrailjevu, te ga razbi ljuto.
6 Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Jer Fekaj sin Remalijin pobi sto i dvadeset tisuæa Judejaca u jedan dan, sve hrabrijeh ljudi, jer ostaviše Gospoda Boga otaca svojih.
7 Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
I Zihrije junak od Jefrema ubi Masiju sina careva i Azrikama upravitelja dvorskoga i Elkanu drugoga do cara.
8 Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
I zarobiše sinovi Izrailjevi braæi svojoj dvjesta tisuæa žena i sinova i kæeri; i zaplijeniše velik plijen od njih, i odnesoše plijen u Samariju.
9 Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
A ondje bijaše prorok Gospodnji po imenu Odid, i izide pred vojsku koja iðaše u Samariju, i reèe im: gle, Gospod Bog otaca vaših razgnjevi se na Judejce, zato ih dade u vaše ruke, te ih pobiste ljuto da do neba doprije.
10 Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
I još mislite podvræi sinove Judine i Jerusalimske da vam budu robovi i robinje; a nijeste li i vi sami skrivili Gospodu Bogu svojemu?
11 Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
Zato poslušajte me sada, i vratite natrag to roblje što zarobiste braæi svojoj, jer se raspalio gnjev Gospodnji na vas.
12 Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
Tada ustaše poglavari sinova Jefremovijeh: Azarija sin Joananov, Varahija sin Mesilemotov i Jezekija sin Salumov i Amasa sin Adlajev na one što se vraæahu s vojske,
13 Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
I rekoše im: neæete dovesti ovamo toga roblja, jer bi nam bilo na grijeh pred Gospodom što vi mislite domeæuæi na grijehe naše i na krivice naše, jer je velika krivica na nama i gnjev se raspalio na Izrailja.
14 Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
I ostaviše vojnici roblje i plijen svoj pred knezovima i svijem zborom.
15 Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
I ustaše ljudi imenovani i uzeše roblje, i sve gole izmeðu njih odješe iz plijena; a kad ih odješe i obuše, nahraniše ih i napojiše i namazaše, i odvedoše na magarcima sve iznemogle, i dovedoše ih u Jerihon grad gdje ima mnogo palama, k braæi njihovoj, pa se vratiše u Samariju.
16 Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
U to vrijeme posla car Ahaz k carevima Asirskim da mu pomogu.
17 Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
Jer još i Idumejci doðoše i razbiše Judu i odvedoše roblje;
18 Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
I Filisteji udariše na gradove po ravni i na južnom kraju Judinu, i uzeše Vet-Semes, i Ejalon i Gedirot i Sohot i sela njegova i Tamnu i sela njezina i Gimzon i sela njegova, i naseliše se u njima.
19 Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
Jer Gospod obaraše Judu s Ahaza cara Izrailjeva, jer odvuèe Judu da grdno griješi Gospodu.
20 Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
I doðe k njemu Telgat-Felnasar car Asirski, i ojadi ga a ne utvrdi.
21 Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
Jer Ahaz uze dio iz doma Gospodnjega i iz doma carskoga i od knezova, i dade caru Asirskom, ali mu ne pomože.
22 Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
I kad bijaše u nevolji, on još veæma griješaše Gospodu; taki bijaše car Ahaz.
23 Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
I prinošaše žrtve bogovima Damaštanskim, koji ga razbiše, i govoraše: kad bogovi careva Sirskih njima pomažu, prinosiæu njima žrtve da bi mi pomagali; ali mu oni biše na to da padne on i sav Izrailj.
24 Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
A Ahaz pokupi sudove doma Božijega, i izlomi sudove doma Božijega, i zatvori vrata doma Gospodnjega i naèini sebi oltare po svijem uglovima u Jerusalimu.
25 Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
I u svakom gradu Judinu naèini visine da kadi bogovima tuðim; i gnjevi Gospoda Boga otaca svojih.
26 Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
A ostala djela njegova i svi putovi njegovi prvi i pošljednji, eto zapisani su u knjizi o carevima Judinijem i Izrailjevijem.
27 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I poèinu Ahaz kod otaca svojih i pogreboše ga u gradu Jerusalimu; ali ga ne metnuše u grob careva Izrailjevijeh. I zacari se na njegovo mjesto Jezekija sin njegov.

< 2 Mbiri 28 >