< 1 Mafumu 13 >

1 Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani.
A gle, èovjek Božji doðe iz zemlje Judine s rijeèju Gospodnjom u Vetilj, kad Jerovoam stajaše kod oltara da kadi.
2 Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’”
I povika put oltara rijeèju Gospodnjom govoreæi: oltare! oltare! Ovako veli Gospod: evo, rodiæe se sin domu Davidovu po imenu Josija, koji æe na tebi klati sveštenike visina, koji kade na tebi, i ljudske æe kosti spaliti na tebi.
3 Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”
I uèini znak istoga dana govoreæi: ovo je znak da je Gospod to rekao: eto, oltar æe se raspasti, i prosuæe se pepeo što je na njemu.
4 Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza.
A kad car Jerovoam èu rijeèi èovjeka Božijega koje vikaše oltaru Vetiljskom, pruži ruku svoju s oltara govoreæi: držite ga! Ali usahnu mu ruka koju pruži na nj, i ne mogaše je povratiti k sebi.
5 Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.
A oltar se raspade, i prosu se pepeo s oltara po znaku koji uèini èovjek Božji rijeèju Gospodnjom.
6 Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.
Tada car reèe èovjeku Božijemu: pripadni ka Gospodu Bogu svojemu, i pomoli se za me da mi se povrati ruka. I èovjek se Božji pomoli Gospodu, i povrati se caru ruka i posta kao što je bila.
7 Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”
I reèe car èovjeku Božijemu: hodi sa mnom kuæi mojoj, i potkrijepi se, i daæu ti dar.
8 Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno.
Ali èovjek Božji reèe caru: da mi daš po kuæe svoje, ne bih išao s tobom niti bih jeo hljeba ni vode pio u ovom mjestu.
9 Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’”
Jer mi je tako zapovjedio svojom rijeèju Gospod govoreæi: ne jedi hljeba ni pij vode, niti se vraæaj istijem putem kojim otideš.
10 Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.
I otide drugim putem, a ne vrati se onijem kojim bješe došao u Vetilj.
11 Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu.
A u Vetilju življaše jedan star prorok, kojemu doðe sin njegov i pripovjedi sve što uèini prorok Božji onaj dan u Vetilju, i rijeèi koje reèe caru; i pripovjediše sinovi toga proroka ocu svojemu.
12 Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera.
A otac im reèe: kojim je putem otišao? I pokazaše sinovi put kojim otide èovjek Božji koji bješe došao iz zemlje Judine.
13 Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo
A on reèe sinovima svojim: osamarite mi magarca. I osamariše mu magarca, te usjede na nj.
14 ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?” Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”
I poðe za èovjekom Božjim, i naðe ga a on sjedi pod hrastom, pa mu reèe: jesi li ti èovjek Božji što doðe iz zemlje Judine? On mu odgovori: ja sam.
15 Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”
A on mu reèe: hodi sa mnom mojoj kuæi da jedeš hljeba.
16 Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno.
Ali on odgovori: ne mogu se vratiti s tobom ni iæi s tobom; niti æu jesti hljeba ni piti vode s tobom u ovom mjestu.
17 Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’”
Jer mi je reèeno rijeèju Gospodnjom: ne jedi hljeba ni pij vode ondje, niti se vraæaj putem kojim otideš.
18 Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’” Koma anamunamiza.
A on mu reèe: i ja sam prorok kao ti, i anðeo Gospodnji reèe mi rijeèju Gospodnjom govoreæi: vrati ga sa sobom u svoju kuæu neka jede hljeba i pije vode. Ali mu slaga.
19 Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.
I vrati se s njim, te jede hljeba u njegovoj kuæi i pi vode.
20 Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo.
A kad sjeðahu za stolom, doðe rijeè Gospodnja proroku koji ga bješe vratio;
21 Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.
I povika na èovjeka Božijega koji bješe došao iz zemlje Judine, i reèe: ovako veli Gospod: što nijesi poslušao rijeèi Gospodnje, i nijesi držao zapovijesti koju ti je zapovjedio Gospod Bog tvoj,
22 Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’”
Nego si se vratio i jeo hljeba i pio vode na mjestu za koje ti je rekao: ne jedi hljeba ni pij vode; zato neæe tvoje tijelo doæi u grob tvojih otaca.
23 Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo.
I pošto se prorok kojega bješe vratio najede hljeba i pošto se napi, osamari mu magarca.
24 Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo.
A kad otide, udesi ga lav na putu i zakla ga. I tijelo njegovo ležaše na putu, i magarac stajaše kod njega; takoðer i lav stajaše kod tijela.
25 Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.
I gle, ljudi prolazeæi vidješe tijelo gdje leži na putu i lava gdje stoji kod tijela, i došavši javiše u gradu u kojem življaše stari prorok.
26 Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”
A kad to èu prorok koji ga bješe vratio s puta, reèe: ono je èovjek Božji, koji ne posluša rijeèi Gospodnje, zato ga dade Gospod lavu da ga rastrgne i usmrti po rijeèi Gospodnjoj koju mu reèe.
27 Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi.
I reèe sinovima svojim govoreæi: osamarite mi magarca. I osamariše.
28 Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo.
I otišav naðe tijelo gdje leži na putu, i magarca i lava gdje stoje kod tijela: lav ne bješe izjeo tijela ni magarca rastrgao.
29 Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda.
Tada prorok podiže tijelo èovjeka Božijega, i metnuv ga na magarca odnese ga natrag, i doðe u grad stari prorok da ga ožali i pogrebe.
30 Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”
I metnu tijelo u svoj grob, i plakahu nad njim govoreæi: jaoh brate!
31 Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake.
A pošto ga pogrebe, reèe sinovima svojim govoreæi: kad umrem, pogrebite me u grobu gdje je pogreben èovjek Božji, pokraj kostiju njegovijeh metnite kosti moje.
32 Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”
Jer æe se zacijelo zbiti što je oglasio po rijeèi Gospodnjoj za oltar Vetiljski i za sve kuæe visina koje su po gradovima Samarijskim.
33 Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe.
Pošto ovo bi, opet se Jerovoam ne vrati sa svojega zloga puta; nego opet naèini iz prostoga naroda sveštenike visinama; ko god hoæaše, tome on posveæivaše ruke i taj postajaše sveštenik visinama.
34 Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.
I to bi na grijeh domu Jerovoamovu da bi se istrijebio i da bi ga nestalo sa zemlje.

< 1 Mafumu 13 >