< 2 Mafumu 1 >

1 Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
A po smrti Ahavovoj odmetnuše se Moavci od Izrailja.
2 Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
A Ohozija pade kroz rešetku iz gornje sobe svoje u Samariji, i razbolje se; pa posla poslanike i reèe im: idite, pitajte Velzevula boga Akaronskoga hoæu li ozdraviti od ove bolesti.
3 Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
Ali anðeo Gospodnji reèe Iliji Tesviæaninu: ustani, izidi na susret poslanicima cara Samarijskoga i reci im: eda li nema Boga u Izrailju, te idete da pitate Velzevula boga u Akaronu?
4 Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
A zato ovako veli Gospod: neæeš se dignuti sa postelje na koju si legao, nego æeš umrijeti. Potom otide Ilija.
5 Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
A sluge se vratiše k Ohoziji, i on im reèe: što ste se vratili?
6 Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
A oni mu rekoše: srete nas jedan èovjek, i reèe nam: idite, vratite se k caru koji vas je poslao, i recite mu: ovako veli Gospod: eda li nema Boga u Izrailju, te šalješ da pitaš Velzevula boga u Akaronu? Zato neæeš se dignuti s postelje na koju si legao, nego æeš umrijeti.
7 Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
A on im reèe: kakav bješe na oèi taj èovjek koji vas srete i to vam reèe?
8 Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
A oni mu odgovoriše: bješe sav kosmat i opasan kožnijem pojasom. A on reèe: to je Ilija Tesviæanin.
9 Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
Tada posla k njemu pedesetnika s njegovom pedesetoricom; i on otide k njemu; i gle, on sjeðaše navrh gore; i pedesetnik mu reèe: èovjeèe Božji, car je zapovjedio, siði.
10 Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
A Ilija odgovarajuæi reèe pedesetniku: ako sam èovjek Božji, neka siðe oganj s neba i proždre tebe i tvoju pedesetoricu. I siðe oganj s neba i proždrije njega i njegovu pedesetoricu.
11 Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
Opet posla k njemu drugog pedesetnika s njegovom pedesetoricom, koji progovori i reèe mu: èovjeèe Božji, car je tako zapovjedio, siði brže.
12 Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
A Ilija odgovori i reèe im: ako sam èovjek Božji, neka siðe oganj s neba i proždre tebe i tvoju pedesetoricu. I siðe oganj Božji s neba i proždrije njega i njegovu pedesetoricu.
13 Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
Tada opet posla treæega pedesetnika s njegovom pedesetoricom. A ovaj treæi pedesetnik kad doðe, kleèe na koljena svoja pred Ilijom, i moleæi ga reèe mu: èovjeèe Božji, da ti je draga duša moja i duša ove pedesetorice, sluga tvojih.
14 Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
Eto, sišao je oganj s neba i proždro prva dva pedesetnika s njihovom pedesetoricom; ali sada da ti je draga duša moja.
15 Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
A anðeo Gospodnji reèe Iliji: idi s njim, i ne boj ga se. I usta Ilija i otide s njim k caru.
16 Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
I reèe mu: ovako veli Gospod: zato što si slao poslanike da pitaju Velzevula boga u Akaronu kao da nema Boga u Izrailju da bi ga pitao, neæeš se dignuti s postelje na koju si legao, nego æeš umrijeti.
17 Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
I umrije po rijeèi Gospodnjoj, koju reèe Ilija, a na njegovo se mjesto zacari Joram druge godine carovanja Jorama sina Josafatova nad Judom, jer on nema sina.
18 Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
A ostala djela Ohozijina što je èinio, nijesu li zapisana u dnevniku careva Izrailjevih?

< 2 Mafumu 1 >