< 1 Mafumu 12 >

1 Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse nʼkuti atapita kumeneko kukamulonga ufumu.
Tada otide Rovoam u Sihem: jer se ondje skupi sav Izrailj da ga zacare.
2 Yeroboamu mwana wa Nebati anamva zimenezi. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamuyo akukhala ku Igupto, pakuti atathawa Mfumu Solomoni iyeyo anakakhala ku Igupto.
A Jerovoam sin Navatov, koji još bijaše u Misiru pobjegavši onamo od cara Solomuna, kad èu, on još osta u Misiru.
3 Tsono anthu anayitanitsa Yeroboamu, ndipo iye pamodzi ndi gulu lonse la ku Israeli anapita kwa Rehobowamu ndipo anamuwuza kuti,
Ali poslaše i dozvaše ga. Tako Jerovoam i sav zbor Izrailjev doðoše i rekoše Rovoamu govoreæi:
4 “Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa kwambiri, koma inu chepetsani ntchito yowawa pa ife ndipo peputsani goli lolemetsa limene anatisenzetsa. Mukatero tidzakutumikirani.”
Tvoj je otac metnuo na nas težak jaram; nego ti sada olakšaj ljutu službu oca svojega i teški jaram koji je metnuo na nas, pak æemo ti služiti.
5 Rehobowamu anayankha kuti, “Pitani, ndipo pakatha masiku atatu, mudzabwerenso.” Choncho anthuwo anapitadi.
A on im reèe: idite, pa do tri dana doðite opet k meni. I narod otide.
6 Ndipo Mfumu Rehobowamu anapempha nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira Solomoni abambo ake pamene anali ndi moyo. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu amenewa?”
Tada car Rovoam uèini vijeæe sa starcima koji stajaše pred Solomunom ocem njegovijem dok bijaše živ, i reèe: kako svjetujete da odgovorim narodu?
7 Iwo anayankha kuti, “Ngati lero mudzakhala mtumiki wa anthu amenewa ndi kuwatumikira ndipo mukawayankha bwino, iwowo adzakhala atumiki anu nthawi zonse.”
A oni mu odgovoriše govoreæi: ako danas ugodiš narodu i poslušaš ih i odgovoriš im lijepijem rijeèima, oni æe ti biti sluge svagda.
8 Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakuluwo anamupatsa ndipo anafunsira nzeru kwa anyamata anzake amene anakulira nawo limodzi omwe ankamutumikira.
Ali on ostavi svjet što ga svjetovaše starci, i uèini vijeæe s mladiæima, koji odrastoše s njim i koji stajahu pred njim.
9 Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ngotani? Kodi ndiwayankhe chiyani anthu amene akunena kwa ine kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anatisenzetsa’?”
I reèe im: šta vi svjetujete da odgovorimo narodu, koji mi rekoše govoreæi: olakšaj jaram koji je metnuo na nas tvoj otac?
10 Anyamata anzake amene anakula nawo limodzi aja anamuyankha kuti, “Anthu amene ananena kwa iwe kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa, koma inu peputsani goli lathu,’ uwawuze kuti ‘Chala changa chakanise nʼchachikulu kupambana chiwuno cha abambo anga.
Tada mu odgovoriše mladiæi koji odrastoše s njim, i rekoše: ovako kaži narodu što ti reèe: tvoj je otac metnuo na nas težak jaram, nego nam ti olakšaj; ovako im reci: moj je mali prst deblji od bedara oca mojega.
11 Abambo anga ankakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzachititsa kuti likhale lolemera kwambiri. Abambo anga ankakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
Otac je moj metnuo na vas težak jaram, a ja æu još dometnuti na vaš jaram; otac vas je moj šibao bièevima, a ja æu vas šibati bodljivijem bièevima.
12 Patapita masiku atatu, Yeroboamu pamodzi ndi anthu onse anabwera kwa Rehobowamu, monga momwe inanenera mfumu kuti, “Mudzabwere pakatha masiku atatu.”
A treæi dan doðe Jerovoam i sav narod k Rovoamu, kako im bješe kazao car rekavši: doðite opet k meni do tri dana.
13 Mfumuyo inawayankha anthuwo mwankhanza. Kukana malangizo amene akuluakulu anayipatsa.
I car odgovori oštro narodu ostavivši svjet što ga svjetovaše starci;
14 Anatsatira malangizo amene anyamata anzake anamupatsa ndipo anati “Abambo anga ankakusenzetsani goli lolemetsa. Ine ndidzachititsa kuti likhale lolemera kwambiri. Abambo anga ankakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
I reèe im kako ga svjetovaše mladiæi govoreæi: moj je otac metnuo na vas težak jaram, a ja æu još dometnuti na jaram vaš; otac vas je moj šibao bièevima, a ja æu vas šibati bodljivijem bièevima.
15 Choncho mfumu sinamvere pempho la anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Yehova, kukwaniritsa mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
I car ogluši se naroda, jer Gospod bješe tako uredio da bi potvrdio rijeè svoju što je rekao preko Ahije Silomljanina Jerovoamu sinu Navatovu.
16 Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kumva zopempha zawo, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, ndi gawo lanjinso mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli, bwererani ku matenti anu! Ziyangʼanira nyumba yako, Iwe Davide!” Kotero Aisraeli anachoka napita ku nyumba zawo.
A kad vidje sav Izrailj gdje ih se car ogluši, odgovori narod caru govoreæi: kakav dio mi imamo s Davidom? nemamo našljedstva sa sinom Jesejevijem. U šatore svoje, Izrailju! a ti Davide, sad gledaj svoju kuæu. Tako otide Izrailj u šatore svoje.
17 Koma Aisraeli amene ankakhala mʼmizinda ya Yuda ankalamuliridwa ndi Rehobowamu.
Samo nad sinovima Izrailjevijem, koji življahu po gradovima Judinijem, zacari se Rovoam.
18 Mfumu Rehobowamu anatuma Adoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli onse anamugeda ndi miyala mpaka kumupha. Koma Mfumu Rehobowamu anakwera msangamsanga galeta wake nathawira ku Yerusalemu.
I car Rovoam posla Adorama koji bijaše nad dankom; ali ga sav Izrailj zasu kamenjem, te pogibe; a car Rovoam brže sjede na kola, te pobježe u Jerusalim.
19 Choncho Aisraeli akhala akuwukira nyumba ya Davide mpaka lero lino.
Tako otpade Izrailj od doma Davidova do današnjega dana.
20 Aisraeli onse atamva kuti Yeroboamu wabwerera kuchokera ku Igupto, anatumiza mawu okamuyitana kuti abwere ku msonkhano ndipo anamuyika kukhala mfumu ya Aisraeli onse. Fuko la Yuda lokha ndi lomwe linkatsatira nyumba ya Davide.
I kad èu sav Izrailj da se vratio Jerovoam, poslavši dozvaše ga na skupštinu, i postaviše ga carem nad svijem Izrailjem. Ne prista za domom Davidovijem nijedno pleme osim samoga plemena Judina.
21 Rehobowamu atafika ku Yerusalemu, anasonkhanitsa nyumba yonse ya Yuda ndi fuko la Benjamini, nasankha ankhondo okwanira 180,000, kuti akamenyane ndi nyumba ya Israeli kuti amubwezere Rehobowamu mwana wa Solomoni ufumu wake.
A Rovoam došav u Jerusalim sazva sav dom Judin i pleme Venijaminovo, sto i osamdeset tisuæa odabranijeh vojnika, da zavojšte na dom Izrailjev da povrate carstvo Rovoamu sinu Solomunovu.
22 Koma Mulungu anayankhula ndi Semaya, munthu wa Mulungu kuti,
Ali doðe rijeè Božja Semeju, èovjeku Božijemu, govoreæi:
23 “Nena kwa Rehobowamu mwana wa Solomoni mfumu ya Yuda, kwa nyumba yonse ya Yuda ndi Benjamini, ndiponso kwa anthu ena onse kuti,
Kaži Rovoamu sinu Solomunovu caru Judinu i svemu domu Judinu i Venijaminovu i ostalome narodu, i reci:
24 ‘Yehova akuti: Musapite kukamenyana ndi abale anu Aisraeli. Aliyense wa inu abwerere kwawo, pakuti zimenezi ndachita ndine.’” Choncho anthuwo anamvera mawu a Yehova ndi kubwerera kwawo, monga analamulira Yehova.
Ovako veli Gospod: ne idite, i ne bijte se s braæom svojom, sinovima Izrailjevijem; vratite se svak svojoj kuæi, jer sam ja naredio tako da bude. I oni poslušaše rijeè Gospodnju i vrativši se otidoše kako Gospod reèe.
25 Tsono Yeroboamu anamanga mzinda wa Sekemu mʼdziko la mapiri la Efereimu ndipo anakhala kumeneko. Kuchokera kumeneko anapita kukamanga mzinda wa Penueli.
Potom sazida Jerovoam Sihem u gori Jefremovoj i naseli se u njemu; a poslije otide odande i sazida Fanuil.
26 Yeroboamu anaganiza mu mtima mwake kuti, “Ndithu, ufumuwu udzabwereranso ku nyumba ya Davide.
I reèe Jerovoam u srcu svom: može se carstvo povratiti domu Davidovu.
27 Ngati anthuwa azipitabe kukapereka nsembe ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu, adzayambanso kutsatira mbuye wawo Rehobowamu, mfumu ya Yuda. Adzandipha ndi kubwerera kwa Mfumu Rehobowamu.”
Ako ovaj narod stane iæi u Jerusalim da prinosi žrtve u domu Gospodnjem, srce æe se narodu obratiti ka gospodaru njegovu Rovoamu caru Judinu, te æe me ubiti, i povratiæe se k Rovoamu caru Judinu.
28 Itapempha nzeru, mfumuyo inapanga mafano awiri a ana angʼombe. Mfumuyo inati kwa anthuwo, “Mwakhala mukupita ku Yerusalemu nthawi yayitali. Iwe Israeli, nayi milungu yako imene inakutulutsa mʼdziko la Igupto.”
Zato car smisli, te naèini dva teleta od zlata, pa reèe narodu: ne treba više da idete u Jerusalim; evo bogova tvojih, Izrailju, koji su te izveli iz zemlje Misirske.
29 Fano lina analiyika ku Beteli ndipo lina analiyika ku Dani.
I namjesti jedno u Vetilju a drugo namjesti u Danu.
30 Ndipo zimenezi zinachimwitsa anthu pakuti anthu ankapita mpaka ku Dani kukapembedza fano limene linali kumeneko.
I to bi na grijeh, jer narod iðaše k jednome do Dana.
31 Yeroboamu anamanga Nyumba za Mulungu pa malo azipembedzo nasankha ansembe kuchokera pakati pa anthu wamba, ngakhale sanali Alevi.
I naèini kuæu na visini, i postavi sveštenike od prostoga naroda koji ne bijahu od sinova Levijevih.
32 Iye anakhazikitsa chikondwerero pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, lofanana ndi tsiku la chikondwerero cha ku Yuda, ndipo ankapereka nsembe pa guwa. Izi ankachita ku Beteli, kupereka nsembe kwa ana angʼombe amene anapanga. Ndipo ku Beteliko anayikako ansembe pa malo achipembedzo amene anamanga.
I uèini Jerovoam praznik osmoga mjeseca petnaestoga dana, kao što je praznik u zemlji Judinoj, i prinese žrtve na oltaru; tako uèini i u Vetilju prinoseæi žrtve teocima koje naèini; i postavi u Vetilju sveštenike visinama koje naèini.
33 Tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chitatu, mwezi umene anawusankha yekha, anapereka nsembe pa guwa limene analimanga ku Beteli. Motero anakhazikitsa chikondwerero cha Aisraeli ndipo iye ankapita kukapereka nsembe yofukiza lubani pa guwa.
I petnaestoga dana osmoga mjeseca, koji bješe smislio u srcu svom, prinošaše žrtve na oltaru koji naèini u Vetilju, i praznovaše praznik sa sinovima Izrailjevijem, i pristupi k oltaru da kadi.

< 1 Mafumu 12 >