< Zekariya 1 >

1 Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
In the eighth month, in the second year of Darius, the word of Jehovah came to Zechariah the son of Berechiah, the son of Iddo, the prophet, saying,
2 “Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
Jehovah was greatly displeased with your fathers.
3 Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Therefore say thou to them, Thus says Jehovah of hosts: Return to me, says Jehovah of hosts, and I will return to you, says Jehovah of hosts.
4 Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
Be ye not as your fathers, to whom the former prophets cried, saying, Thus says Jehovah of hosts: Return ye now from your evil ways, and from your evil doings, but they did not hear, nor hearken to me, says Jehovah.
5 Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
Your fathers, where are they? And the prophets, do they live forever?
6 Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
But my words and my statutes, which I commanded my servants the prophets, did they not overtake your fathers? And they turned and said, Like as Jehovah of hosts thought to do to us, according to our ways, and according to our doings, so he has dealt with us.
7 Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
Upon the twenty-fourth day of the eleventh month, which is the month Shebat, in the second year of Darius, the word of Jehovah came to Zechariah the son of Berechiah, the son of Iddo, the prophet, saying,
8 Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
I saw in the night, and, behold, a man riding upon a red horse, and he stood among the myrtle trees that were in the bottom. And behind him there were horses, red, sorrel, and white.
9 Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
Then I said, O my lord, what are these? And the agent who talked with me said to me, I will show thee what these are.
10 Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
And the man who stood among the myrtle trees answered and said, These are they whom Jehovah has sent to walk to and fro through the earth.
11 Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
And they answered the agent of Jehovah who stood among the myrtle trees, and said, We have walked to and fro through the earth, and, behold, all the earth sits still, and is at rest.
12 Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
Then the agent of Jehovah answered and said, O Jehovah of hosts, how long will thou not have mercy on Jerusalem and on the cities of Judah, against which thou have had indignation these seventy years?
13 Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
And Jehovah answered the agent who talked with me with good words, comforting words.
14 Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
So the agent who talked with me said to me, Cry thou, saying, Thus says Jehovah of hosts: I am jealous for Jerusalem and for Zion with a great jealousy.
15 koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
And I am very greatly displeased with the nations that are at ease. For I was but a little displeased, and they helped forward the affliction.
16 “Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Therefore thus says Jehovah: I have returned to Jerusalem with mercies. My house shall be built in it, says Jehovah of hosts, and a line shall be stretched forth over Jerusalem.
17 “Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
Cry yet again, saying, Thus says Jehovah of hosts: My cities shall yet overflow with prosperity, and Jehovah shall yet comfort Zion, and shall yet choose Jerusalem.
18 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
And I lifted up my eyes, and saw, and, behold, four horns.
19 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
And I said to the agent who talked with me, What are these? And he answered me, These are the horns which have scattered Judah, Israel, and Jerusalem.
20 Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
And Jehovah showed me four smiths.
21 Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”
Then I said, What are these coming to do? And he spoke, saying, These are the horns which scattered Judah, so that no man lifted up his head. But these have come to terrify them, to cast down the horns of the nations, which lifted up their horn against the land of Judah to scatter it.

< Zekariya 1 >