< Hagai 2 >

1 Pa tsiku la 21 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Yehova anayankhula kudzera mwa mneneri Hagai kuti:
In the seventh month, in the twenty-first day of the month, the word of Jehovah came by Haggai the prophet, saying,
2 “Yankhula kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa anthu onse otsala. Afunse kuti,
Speak now to Zerubbabel the son of Shealtiel, governor of Judah, and to Joshua the son of Jehozadak, the high priest, and to the remnant of the people, saying,
3 ‘Kodi alipo amene watsala pakati panu amene anaona ulemerero wakale wa Nyumba iyi? Nanga tsopano ikuoneka motani kwa inu? Kodi sikuoneka ngati yopanda pake kwa inu?
Who is left among you that saw this house in its former glory? And how do ye see it now? Is it not in your eyes as nothing?
4 Iwe Zerubabeli, limba mtima tsopano,’ akutero Yehova. ‘Limba mtima, iwe Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe. Limbani mtima, anthu nonse a mʼdziko,’ akutero Yehova, ‘ndipo gwirani ntchito. Pakuti ine ndili nanu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Yet now be strong, O Zerubbabel, says Jehovah, and be strong, O Joshua, son of Jehozadak, the high priest, and be strong, all ye people of the land, says Jehovah, and work. For I am with you, says Jehovah of hosts,
5 ‘Izi ndi zimene ndinapangana nanu pamene munkatuluka ku Igupto. Ndipo Mzimu wanga uli pakati panu. Musachite mantha.’
according to the word that I covenanted with you when ye came out of Egypt, and my Spirit abode among you. Fear ye not.
6 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakapita nthawi pangʼono ndidzagwedezanso thambo ndi dziko lapansi, nyanja ndi mtunda.
For thus says Jehovah of hosts: Yet once, it is a little while, and I will shake the heavens, and the earth, and the sea, and the dry land.
7 Ndidzagwedeza mitundu yonse ya anthu, ndipo chimene mitundu yonse ya anthu imachifuna chidzabwera, ndipo ndidzaza Nyumba ino ndi ulemerero,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
And I will shake all nations, and the precious things of all nations shall come, and I will fill this house with glory, says Jehovah of hosts.
8 ‘Siliva yense ndi wanga, golide yense ndi wanganso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
The silver is mine, and the gold is mine, says Jehovah of hosts.
9 ‘Ulemerero wa nyumba iyi udzaposa ulemerero wa nyumba yoyamba ija,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo pamalo pano ndidzakhazikitsapo mtendere,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
The latter glory of this house shall be greater than the former, says Jehovah of hosts, and in this place I will give peace, says Jehovah of hosts.
10 Chaka chachiwiri cha Dariyo, pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti:
In the twenty-fourth day of the ninth month, in the second year of Darius, the word of Jehovah came by Haggai the prophet, saying,
11 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Funsa ansembe za zimene lamulo likunena:
Thus says Jehovah of hosts: Ask now the priests concerning the law, saying,
12 Ngati munthu wakulunga nyama yopatulika mu mkanjo wake, ndipo mkanjowo nʼkukhudza buledi kapena msuzi, kapena vinyo, mafuta kapena chakudya cha mtundu wina uliwonse, kodi zimenezo zimasanduka zopatulika?’” Ansembe anayankha kuti, “Ayi.”
If a man bears holy flesh in the skirt of his garment, and with his skirt touches bread, or pottage, or wine, or oil, or any food, shall it become holy? And the priests answered and said, No.
13 Pamenepo Hagai anati, “Ngati munthu amene anayipitsidwa pokhudza mtembo akhudza chimodzi cha zinthu zimenezi, kodi chinthucho chimayipitsidwa?” Ansembe anayankha kuti, “Inde, chimayipitsidwa.”
Then Haggai said, If a man who is unclean because of a dead body touches any of these, shall it be unclean? And the priests answered and said, It shall be unclean.
14 Pamenepo Hagai anati, “‘Ndi mmene zilili ndi anthu awa ndi dziko ili pamaso panga,’ akutero Yehova. ‘Chilichonse amachita ndiponso chilichonse chimene amapereka nʼchodetsedwa.
Then Haggai answered and said, So is this people, and so is this nation before me, says Jehovah, and so is every work of their hands. And that which they offer there is unclean.
15 “‘Tsopano muganizire zimenezi kuyambira lero mpaka mʼtsogolo. Ganizirani momwe zinthu zinalili asanayambe kumanga nyumba ya Yehova.
And now, I pray you, consider from this day and backward, before a stone was laid upon a stone in the temple of Jehovah.
16 Pamene munthu ankayembekezera miyeso ya tirigu makumi awiri ankangopeza khumi yokha. Munthu akapita kuti akatunge miyeso makumi asanu ya vinyo mu mtsuko, ankangopeza miyeso makumi awiri yokha.
Through all that time, when a man came to a heap of twenty measures, there were but ten. When he came to the wine vat to draw out fifty vessels, there were but twenty.
17 Ndinawononga ntchito yonse ya manja anu ndi chinsikwi, chiwawu ndi matalala, komabe inu simunatembenukire kwa Ine,’ akutero Yehova
I smote you with blasting and with mildew and with hail in all the work of your hands, yet ye turned not to me, says Jehovah.
18 ‘Kuyambira lero tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi mpaka mʼtsogolo, chonde ganizirani bwino tsiku limene munayika maziko a nyumba ya Yehova. Ganizirani bwino.
Consider, I pray you, from this day and backward, from the twenty-fourth day of the ninth month, since the day that the foundation of Jehovah's temple was laid, consider it.
19 Kodi mʼnkhokwe mwatsala mbewu? Mpaka lero, mpesa ndi mtengo wa mkuyu, makangadza ndi mtengo wa olivi sizinabereke zipatso. “‘Kuyambira lero mpaka mʼtsogolo ndidzakudalitsani.’”
Is the seed yet in the barn? Yea, the vine, and the fig tree, and the pomegranate, and the olive tree have not brought forth. From this day I will bless you.
20 Yehova anayankhula ndi Hagai kachiwiri, pa tsiku la 24 la mwezi kuti:
And the word of Jehovah came the second time to Haggai in the twenty-fourth day of the month, saying,
21 “Uza Zerubabeli, bwanamkubwa wa Yuda, kuti ndidzagwedeza thambo ndi dziko lapansi.
Speak to Zerubbabel, governor of Judah, saying, I will shake the heavens and the earth.
22 Ndidzagwetsa mipando yaufumu ndi kuwononga mphamvu za maufumu achilendo. Ndidzagubuduza magaleta ndi okwerapo ake; akavalo ndi okwerapo ake adzagwa, aliyense adzaphedwa ndi lupanga la mʼbale wake.
And I will overthrow the throne of kingdoms, and I will destroy the strength of the kingdoms of the nations. And I will overthrow the chariots, and those who ride in them. And the horses and their riders shall come down, each one by the sword of his brother.
23 “‘Tsiku limenelo,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndidzakutenga, iwe mtumiki wanga Zerubabeli mwana wa Sealatieli,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakusandutsa kukhala mphete yanga yolamulira, pakuti ndasankha iwe,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
In that day, says Jehovah of hosts, I will take thee, O Zerubbabel, my servant, the son of Shealtiel, says Jehovah, and will make thee as a signet. For I have chosen thee, says Jehovah of hosts.

< Hagai 2 >