< Zekariya 2 >

1 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
And I lifted up my eyes, and looked. And, behold, a man with a measuring line in his hand.
2 Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
Then I said, Where do thou go? And he said to me, To measure Jerusalem. To see what is the breadth of it, and what is the length of it.
3 Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
And, behold, the agent who talked with me went forth. And another agent went out to meet him,
4 ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
and said to him, Run, speak to this young man, saying, Jerusalem shall be inhabited as villages without walls, because of the multitude of men and cattle therein.
5 Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
For I, says Jehovah, will be to her a wall of fire round about, and I will be the glory in the midst of her.
6 “Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
Ho, ho, flee from the land of the north, says Jehovah. For I have spread you abroad as the four winds of the heavens, says Jehovah.
7 “Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
Ho Zion, escape, thou who dwell with the daughter of Babylon.
8 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
For thus says Jehovah of hosts: After glory he has sent me to the nations which plundered you. For he who touches you touches the apple of his eye.
9 Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
For, behold, I will shake my hand over them, and they shall be a spoil to those who served them. And ye shall know that Jehovah of hosts has sent me.
10 “Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
Sing and rejoice, O daughter of Zion, for, lo, I come, and I will dwell in the midst of thee, says Jehovah.
11 “Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
And many nations shall join themselves to Jehovah in that day, and shall be my people, and I will dwell in the midst of thee. And thou shall know that Jehovah of hosts has sent me to thee.
12 Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
And Jehovah shall inherit Judah as his portion in the holy land, and shall yet choose Jerusalem.
13 Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”
Be silent, all flesh, before Jehovah, for he has arisen out of his holy habitation.

< Zekariya 2 >