< Masalimo 76 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
In Judah God is known. His name is great in Israel.
2 Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
In Salem also is his tabernacle, and his dwelling-place in Zion.
3 Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
There he broke the arrows of the bow, the shield, and the sword, and the battle. (Selah)
4 Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
Thou are more glorious and excellent than the mountains of prey.
5 Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
The stouthearted are made a spoil. They have slept their sleep, and none of the men of might have found their hands.
6 Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
At thy rebuke, O God of Jacob, both chariot and horse are cast into a deep sleep.
7 Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
Thou, even thou, are to be feared. And who may stand in thy sight when once thou are angry?
8 Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
Thou caused sentence to be heard from heaven. The earth feared and was still
9 pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
when God arose to judgment, to save all the meek of the earth. (Selah)
10 Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
Surely the inward thought of man shall praise thee, even the residue of inward thought will observe a festival to thee.
11 Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
Vow, and pay to Jehovah your God. Let all who are round about him bring presents to him who ought to be feared.
12 Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.
He will cut off the spirit of rulers. He is fearful to the kings of the earth.

< Masalimo 76 >