< Masalimo 71 >

1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
In thee, O Jehovah, do I take refuge. Let me never be put to shame.
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
Deliver me in thy righteousness, and rescue me. Bow down thine ear to me, and save me.
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Be thou to me a rock of habitation to which I may continually resort. Thou have given commandment to save me, for thou are my rock and my fortress.
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
Rescue me, O my God, out of the hand of a wicked man, out of the hand of an unrighteous and cruel man.
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
For thou are my hope, O lord Jehovah, my trust from my youth.
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
By thee I have been held up from the womb. Thou are he who took me out of my mother's bowels. My praise shall be continually of thee.
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
I am as a wonder to many, but thou are my strong refuge.
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
My mouth shall be filled with thy praise, and with thy honor all the day.
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
Cast me not off in the time of old age. Forsake me not when my strength fails.
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
For my enemies speak concerning me, and those who watch for my soul take counsel together,
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
saying, God has forsaken him. Pursue and take him, for there is none to deliver.
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
O God, be not far from me. O my God, make haste to help me.
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
Let them be put to shame and consumed who are adversaries to my soul. Let them be covered with reproach and dishonor who seek my hurt.
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
But I will hope continually, and will praise thee yet more and more.
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
My mouth shall tell of thy righteousness, of thy salvation all the day, for I know not the numbers.
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
I will come with the mighty acts of the lord Jehovah. I will make mention of thy righteousness, even of thine only.
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
O God, thou have taught me from my youth, and I have declared thy wondrous works until now.
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
Yea, even when I am old and gray headed, O God, forsake me not, until I have declared thy strength to a generation, thy might to everyone who is to come.
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
Thy righteousness also, O God, is very high, thou who have done great things. O God, who is like thee?
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
Thou, who have shown us many and great troubles, will revive us again, and will bring us up again from the depths of the earth.
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
Increase thou my greatness, and turn again and comfort me.
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
I will also praise thee with the psaltery, even thy truth, O my God. To thee I will sing praises with the harp, O thou Holy One of Israel.
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
My lips shall shout for joy when I sing praises to thee, and my soul, which thou have redeemed.
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
My tongue also shall talk of thy righteousness all the day long. For they are put to shame, for they are confounded, who seek my hurt.

< Masalimo 71 >