< Masalimo 67 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
God be merciful to us, and bless us, and cause his face to shine upon us (Selah)
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
that thy way may be known upon earth, thy salvation among all nations.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the peoples praise thee, O God. Let all the peoples praise thee.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
O let the nations be glad and sing for joy. For thou will judge the peoples with equity, and govern the nations upon earth. (Selah)
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the peoples praise thee, O God. Let all the peoples praise thee.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
The earth has yielded its increase. God, even our own God, will bless us.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
God will bless us, and all the ends of the earth shall fear him.

< Masalimo 67 >