< Masalimo 64 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
Hear my voice, O God, in my complaint. Preserve my life from fear of the enemy.
2 Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
Hide me from the secret counsel of evildoers, from the tumult of the workers of iniquity,
3 Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
who have whet their tongue like a sword, and have aimed their arrows, even bitter words,
4 Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
that they may shoot in secret places at a blameless man. Suddenly do they shoot at him, and fear not.
5 Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
They encourage themselves in an evil purpose. They converse of laying snares secretly. They say, Who will see them?
6 Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
They search out iniquities, saying, We have accomplished a diligent search. And the inward part of man and the heart are deep.
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
But God will shoot at them. With an arrow they shall suddenly be wounded.
8 Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
So they shall be made to stumble, their own tongue being against them. All who see them shall wag the head.
9 Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
And all men shall fear. And they shall declare the work of God, and shall wisely consider of his doing.
10 Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!
A righteous man shall be glad in Jehovah, and shall take refuge in him. And all the upright in heart shall glory.

< Masalimo 64 >