< Masalimo 62 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
My soul waits in silence for God only. From him is my salvation.
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
He only is my rock and my salvation, my high tower. I shall not be greatly moved.
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
How long will ye set upon a man, that ye may kill, all of you, like a leaning wall, like a tottering fence?
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
They only consult to thrust him down from his dignity. They delight in lies. They bless with their mouth, but they curse inwardly. (Selah)
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
My soul, wait thou in silence for God only, for my expectation is from him.
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
He only is my rock and my salvation, my high tower. I shall not be moved.
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
With God is my salvation and my glory. The rock of my strength, and my refuge, is in God.
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Trust in him at all times, ye people. Pour out your heart before him. God is a refuge for us. (Selah)
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Surely men of low degree are vanity, and men of high degree are a lie. In the balances they will go up. They are together lighter than vanity.
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Trust not in oppression, and become not vain in robbery. If riches increase, set not your heart on it.
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
God has spoken once, twice I have heard this, that power belongs to God.
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
Also to thee, O Lord, belongs loving kindness, for thou render to every man according to his work.

< Masalimo 62 >