< Masalimo 44 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
We have heard with our ears, O God, our fathers have told us, what work thou did in their days, in the days of old.
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
Thou drove out the nations with thy hand, but thou planted them. Thou afflicted the peoples, but thou spread them abroad.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
For they did not get the land in possession by their own sword, nor did their own arm save them, but thy right hand, and thine arm, and the light of thy countenance, because thou were favorable to them.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
Thou are my King, O God. Command deliverance for Jacob.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
Through thee we will push down our adversaries. Through thy name we will tread them under who rise up against us.
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
For I will not trust in my bow, nor shall my sword save me.
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
But thou have saved us from our adversaries, and have put them to shame who hate us.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
In God we have made our boast all the day long, and we will give thanks to thy name forever. (Selah)
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
But now thou have cast off, and brought us to dishonor, and go not forth with our armies.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
Thou make us to turn back from the adversary. And those who hate us take spoil for themselves.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
Thou have made us like sheep for food, and have scattered us among the nations.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
Thou sell thy people for nothing, and have not increased by their price.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
Thou make us a reproach to our neighbors, a scoffing and a derision to those who are round about us.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
Thou make us a byword among the nations, a shaking of the head among the peoples.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
All the day long my dishonor is before me, and the shame of my face has covered me,
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
for the voice of him who reproaches and blasphemes, because of the enemy and the avenger.
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
All this has come upon us, yet we have not forgotten thee, nor have we dealt falsely in thy covenant.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
Our heart is not turned back, nor have our steps declined from thy way,
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
that thou have greatly broken us in the place of jackals, and covered us with the shadow of death.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
If we have forgotten the name of our God, or spread forth our hands to a strange god,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
will not God search this out? For he knows the secrets of the heart.
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
Yea, for thy sake we are killed all the day long. We are accounted as sheep for the slaughter.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
Awake, why do thou sleep, O Lord? Arise, cast not off forever.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
Why do thou hide thy face, and forget our affliction and our oppression?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
For our soul is bowed down to the dust; our body clings to the ground.
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Rise up for our help, and redeem us for thy loving kindness' sake.

< Masalimo 44 >