< Masalimo 48 >

1 Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
Great is Jehovah, and greatly to be praised in the city of our God, in his holy mountain.
2 Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
Beautiful in elevation, the joy of the whole earth, is mount Zion, on the sides of the north, the city of the great King.
3 Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
God has made himself known in her palaces for a refuge.
4 Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
For, lo, the kings assembled themselves. They passed by together.
5 iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
They saw it, then were they amazed. They were dismayed, they hastened away.
6 Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
Trembling took hold of them there, pain, as of a woman in travail.
7 Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
With the east wind thou break the ships of Tarshish.
8 Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
As we have heard, so we have seen in the city of Jehovah of hosts, in the city of our God, God will establish it forever. (Selah)
9 Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
We have thought on thy loving kindness, O God, in the midst of thy temple.
10 Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
As is thy name, O God, so is thy praise to the ends of the earth. Thy right hand is full of righteousness.
11 Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
Let mount Zion be glad. Let the daughters of Judah rejoice because of thy judgments.
12 Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
Walk about Zion, and go round about her. Number the towers of it,
13 Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
mark ye well her bulwarks, consider her palaces, that ye may tell it to the generation following.
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.
For this God is our God forever and ever. He will be our guide even to death.

< Masalimo 48 >