< Masalimo 39 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide. Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe; ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
I said, I will take heed to my ways, that I sin not with my tongue. I will keep my mouth with a bridle while the wicked man is before me.
2 Koma pamene ndinali chete osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino mavuto anga anachulukirabe.
I was mute with silence. I held my peace, even from good, and my sorrow was stirred.
3 Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga, ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka; kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:
My heart was hot within me. While I was musing the fire burned. Then I spoke with my tongue:
4 “Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga ndi chiwerengero cha masiku anga; mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
Jehovah, make me to know my end, and the measure of my days, what it is. Let me know how frail I am.
5 Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri, kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu; moyo wa munthu aliyense ndi waufupi. (Sela)
Behold, thou have made my days as handbreadths, and my life-time is as nothing before thee. Surely every man at his best condition is altogether vanity. (Selah)
6 Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku: Iye amangovutika koma popanda phindu; amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.
Surely every man walks in a shadow. Surely they are disquieted in vain. He heaps up, and knows not who shall gather them.
7 “Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani? Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
And now, Lord, what do I wait for? My hope is in thee.
8 Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse; musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
Deliver me from all my transgressions. Make me not the reproach of the foolish.
9 Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
I was mute. I opened not my mouth, because thou did it.
10 Chotsani mkwapulo wanu pa ine; ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
Remove thy stroke away from me. I am consumed by the blow of thy hand.
11 Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo; mumawononga chuma chawo monga njenjete; munthu aliyense ali ngati mpweya. (Sela)
When thou have corrected man with rebukes for iniquity, thou make his beauty to disintegrate like a moth. Surely every man is vanity. (Selah)
12 “Imvani pemphero langa Inu Yehova, mverani kulira kwanga kopempha thandizo; musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu, popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa; monga anachitira makolo anga onse.
Hear my prayer, O Jehovah, and give ear to my cry. Keep not silent at my tears, for I am a stranger with thee, a sojourner, as all my fathers were.
13 Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala ndisanafe ndi kuyiwalika.”
O spare me, that I may recover strength before I go from here, and be no more.

< Masalimo 39 >