< Masalimo 38 >

1 Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
O Jehovah, rebuke me not in thy wrath, nor chasten me in thy hot displeasure.
2 Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
For thine arrows stick fast in me, and thy hand presses me severely.
3 Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
There is no soundness in my flesh because of thine indignation, nor is there any health in my bones because of my sin.
4 Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
For my iniquities have gone over my head. As a heavy burden they are too heavy for me.
5 Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
My wounds are loathsome and corrupt, because of my foolishness.
6 Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
I am pained and bowed down greatly. I go mourning all the day long.
7 Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
For my loins are filled with burning, and there is no soundness in my flesh.
8 Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
I am faint and severely bruised. I have groaned because of the disquietness of my heart.
9 Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
Lord, all my desire is before thee, and my groaning is not hid from thee.
10 Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
My heart throbs, my strength fails me. As for the light of my eyes, it also is gone from me.
11 Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
Those I love and my friends stand aloof from my plague, and my kinsmen stand afar off.
12 Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
Those also who seek after my life lay snares for me. And those who seek my hurt speak mischievous things, and meditate deceits all the day long.
13 Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
But I, as a deaf man, hear not. And I am as a mute man who opens not his mouth.
14 Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
Yea, I am as a man who hears not, and in whose mouth are no reproofs.
15 Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
For in thee, O Jehovah, do I hope. Thou will answer, O Lord my God.
16 Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
For I said, Lest they rejoice over me. When my foot slips, they magnify themselves against me.
17 Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
For I am ready to fall, and my sorrow is continually before me.
18 Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
For I will declare my iniquity. I will be sorry for my sin.
19 Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
But my enemies are energetic, and are strong, and those who hate me wrongfully are multiplied.
20 Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
They also who render evil for good are adversaries to me, because I follow the thing that is good.
21 Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
Forsake me not, O Jehovah. O my God, be not far from me.
22 Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.
Make haste to help me, O Lord, my salvation.

< Masalimo 38 >