< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Praise ye Jehovah. I will give thanks to Jehovah with my whole heart, in the council of the upright, and in the congregation.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
The works of Jehovah are great, sought out by all those who have pleasure in it.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
His work is honor and majesty, and his righteousness endures forever.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
He has made his wonderful works to be remembered. Jehovah is gracious and merciful.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
He has given food to those who fear him. He will ever be mindful of his covenant.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
He has shown his people the power of his works, in giving them the heritage of the nations.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
The works of his hands are truth and justice. All his precepts are sure.
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
They are established forever and ever. They are done in truth and uprightness.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
He has sent redemption to his people. He has commanded his covenant forever. Holy and reverend is his name.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
The fear of Jehovah is the beginning of wisdom, and all who act accordingly have a good understanding. His praise endures forever.

< Masalimo 111 >