< Masalimo 110 >

1 Salimo la Davide. Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti, “Khala ku dzanja langa lamanja mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.”
Jehovah says to my Lord, Sit thou at my right hand until I make thine enemies thy footstool.
2 Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni; udzalamulira pakati pa adani ako.
Jehovah will send forth the rod of thy strength out of Zion. Rule thou in the midst of thine enemies.
3 Ankhondo ako adzakhala odzipereka pa tsiku lako la nkhondo. Atavala chiyero chaulemerero, kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha, udzalandira mame a unyamata wako.
Thy people offer themselves willingly in the day of thy power, in holy array. Out of the womb of the morning thou have the dew of thy youth.
4 Yehova walumbira ndipo sadzasintha maganizo ake: “Ndiwe wansembe mpaka muyaya monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”
Jehovah has sworn, and will not repent. Thou are a priest forever after the order of Melchizedek.
5 Ambuye ali kudzanja lako lamanja; Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.
The Lord at thy right hand will strike through kings in the day of his wrath.
6 Adzaweruza anthu a mitundu ina, adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.
He will judge among the nations. He will fill with dead bodies. He will strike through the head in many countries.
7 Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira; choncho adzaweramutsa mutu wake.
He will drink of the brook in the way, therefore he will lift up the head.

< Masalimo 110 >