< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
My heart is fixed, O God, I will sing, yea, I will sing praises, even with my glory.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Awake, psaltery and harp. I myself will awake right early.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
I will give thanks to thee, O Jehovah, among the peoples, and I will sing praises to thee among the nations.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
For thy loving kindness is great above the heavens, and thy truth is to the skies.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Be thou exalted, O God, above the heavens, and thy glory above all the earth.
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
That thy beloved may be delivered, save with thy right hand, and answer us.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
God has spoken in his holiness. I will exult. I will divide Shechem, and mete out the valley of Succoth.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Gilead is mine. Manasseh is mine. Ephraim also is the defense of my head. Judah is my scepter.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moab is my wash pot. Upon Edom I will cast my shoe. Over Philistia I will shout.
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Who will bring me into the fortified city? Who has led me to Edom?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Have thou not cast us off, O God? And thou go not forth, O God, with our armies.
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Give us help against the adversary, for vain is the help of man.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Through God we shall do valiantly, for he it is who will tread down our adversaries.

< Masalimo 108 >