< Miyambo 9 >

1 Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
Wisdom has built her house. She has hewn out her seven pillars.
2 Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
She has killed her beasts. She has mingled her wine. She has also furnished her table.
3 Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
She has sent forth her maidens. She cries out upon the highest places of the city:
4 “Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
He who is simple, let him turn in here. As for him who is void of understanding, she says to him,
5 “Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
Come, eat ye of my bread, and drink of the wine which I have mingled.
6 Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
Forsake ye simpleness, and live, and walk in the way of understanding.
7 Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
He who corrects a scoffer gets himself reviling. And he who reproves a wicked man gets himself a bruise.
8 Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
Reprove not a scoffer, lest he hate thee. Reprove a wise man, and he will love thee.
9 Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
Give opportunity to a wise man, and he will be yet wiser. Teach a righteous man, and he will increase in learning.
10 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
The fear of Jehovah is the beginning of wisdom, and the knowledge of the Holy is understanding.
11 Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
For by me thy days shall be multiplied, and the years of thy life shall be increased.
12 Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
If thou are wise, thou are wise for thyself. And if thou scoff, thou alone shall bear it.
13 Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
The foolish woman is clamorous, simple, and knows nothing.
14 Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
And she sits at the door of her house, on a seat in the high places of the city,
15 kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
to call to those who pass by, who go right on their ways:
16 Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
He who is simple, let him turn in here. And as for him who is void of understanding, she says to him,
17 “Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
Stolen waters are sweet, and bread in secret is pleasant.
18 Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol h7585)
But he knows not that the dead are there, that her guests are in the depths of Sheol. (Sheol h7585)

< Miyambo 9 >