< Miyambo 8 >

1 Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
Does not wisdom cry out, and understanding put forth her voice?
2 Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
On the top of high places by the way, where the paths meet, she stands.
3 Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
Beside the gates, at the entry of the city, at the coming in at the doors, she cries aloud:
4 Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
To you, O men, I call. And my voice is to the sons of men.
5 Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
O ye simple, understand prudence, and, ye fools, be of an understanding heart.
6 Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
Hear, for I will speak excellent things. And the opening of my lips shall be right things.
7 Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
For my mouth shall utter truth. And wickedness is an abomination to my lips.
8 Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
All the words of my mouth are in righteousness. There is nothing crooked or perverse in them.
9 Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
They are all plain to him who understands, and right to those who find knowledge.
10 Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
Receive my instruction, and not silver, and knowledge rather than choice gold.
11 Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
For wisdom is better than rubies, and all the things that may be desired are not to be compared to it.
12 Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
I, wisdom, have made prudence my dwelling, and find out knowledge and discretion.
13 Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
The fear of Jehovah is to hate evil. Pride, and arrogance, and the evil way, and the perverse mouth, do I hate.
14 Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
Counsel is mine, and sound knowledge. I am understanding, I have might.
15 Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
By me kings reign, and rulers decree justice.
16 Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
By me rulers rule, and ranking men, even all the judges of the earth.
17 Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
I love those who love me, and those who seek me diligently shall find me.
18 Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
Riches and honor are with me, durable wealth and righteousness.
19 Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
My fruit is better than gold, yea, than fine gold, and my revenue than choice silver.
20 Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
I walk in the way of righteousness, in the midst of the paths of justice,
21 Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
that I may cause those who love me to inherit substance, and that I may fill their treasuries.
22 “Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
Jehovah possessed me in the beginning of his way, before his works of old.
23 Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
I was set up from everlasting, from the beginning, before the earth was,
24 Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
when there were no depths. I was brought forth when there were no fountains abounding with water,
25 Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
before the mountains were settled, before the hills. I was brought forth
26 lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
while as yet he had not made the earth, nor the fields, nor the beginning of the dust of the world.
27 Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
When he established the heavens, I was there. When he set a circle upon the face of the deep,
28 pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
when he made firm the skies above, when the fountains of the deep became strong,
29 pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
when he gave to the sea its bound that the waters should not transgress his commandment, when he marked out the foundations of the earth,
30 Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
then I was by him, a master workman. And I was daily his delight, rejoicing always before him,
31 Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
rejoicing in his habitable earth. And my delight was with the sons of men.
32 “Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
Now therefore, ye sons, hearken to me. For blessed are those who keep my ways.
33 Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
Hear instruction, and be wise, and do not refuse it.
34 Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
Blessed is the man who hears me, watching daily at my gates, waiting at the posts of my doors.
35 Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
For he who finds me finds life, and shall obtain favor of Jehovah.
36 Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”
But he who sins against me wrongs his own soul. All those who hate me love death.

< Miyambo 8 >