< Miyambo 26 >

1 Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
As snow in summer, and as rain in harvest, so honor is not seemly for a fool.
2 Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
As the sparrow in her wandering, as the swallow in her flying, so the curse that is causeless does not alight.
3 Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
A whip for the horse, a bridle for the donkey, and a rod for the back of fools.
4 Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
Answer not a fool according to his folly, lest thou also be like to him.
5 Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
Answer a fool according to his folly, lest he be wise in his own conceit.
6 Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
He who sends a message by the hand of a fool cuts off the feet, and drinks injury.
7 Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
The legs of a lame man hang loose. So is a proverb in the mouth of fools.
8 Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
As he who binds a stone in a sling, so is he who gives honor to a fool.
9 Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
As a thorn that goes up into the hand of a drunkard, so is a proverb in the mouth of fools.
10 Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
As an archer who wounds all, so is he who hires a fool, and he who hires those who pass by.
11 Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
As a dog who returns to his vomit, is a fool who repeats his folly.
12 Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
See thou a man wise in his own conceit? There is more hope for a fool than of him.
13 Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
The sluggard says, There is a lion in the way; a lion is in the streets.
14 Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
The door turns upon its hinges, so does the sluggard upon his bed.
15 Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
The sluggard buries his hand in the dish. It wearies him to bring it again to his mouth.
16 Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
The sluggard is wiser in his own conceit than seven men who can render a reason.
17 Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
He who passes by, and meddles with strife not his, is like he who takes a dog by the ears.
18 Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
As a madman who casts firebrands, arrows, and death,
19 ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
so is the man who deceives his neighbor, and says, Am I not in sport?
20 Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
For lack of wood the fire goes out, and where there is no whisperer, contention ceases.
21 Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
As coals are to hot embers, and wood to fire, so is a contentious man to inflame strife.
22 Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
The words of a whisperer are as dainty morsels, and they go down into the innermost parts.
23 Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
Fervent lips and a wicked heart are an earthen vessel overlaid with silver dross.
24 Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
He who hates masquerades with his lips, but he lays up deceit within him.
25 Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
When he speaks graciously, believe him not, for there are seven abominations in his heart.
26 Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
Though his hatred cover itself with guile, his wickedness shall be openly shown before the assembly.
27 Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
He who digs a pit shall fall in it, and he who rolls a stone, it shall return upon him.
28 Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.
A lying tongue hates those whom it has wounded, and a flattering mouth works ruin.

< Miyambo 26 >