< Nehemiya 7 >

1 Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
Now it came to pass, when the wall was built, and I had set up the doors, and the porters and the singers and the Levites were appointed,
2 Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
that I gave my brother Hanani, and Hananiah the governor of the castle, charge over Jerusalem, for he was a faithful man, and feared God above many.
3 Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
And I said to them, Let not the gates of Jerusalem be opened until the sun be hot, and while they stand on guard, let them shut the doors, and bar ye them. And appoint watchmen of the inhabitants of Jerusalem, everyone in his watch, and everyone to be opposite his house.
4 Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
Now the city was wide and large, but the people in it were few, and the houses were not built.
5 Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
And my God put into my heart to gather together the ranking men, and the rulers, and the people, that they might be reckoned by genealogy. And I found the book of the genealogy of those who came up at the first. And I found written therein:
6 Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
These are the sons of the province who went up out of the captivity of those who had been carried away, whom Nebuchadnezzar the king of Babylon had carried away, and who returned to Jerusalem and to Judah, everyone to his city,
7 Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
who came with Zerubbabel, Jeshua, Nehemiah, Azariah, Raamiah, Nahamani, Mordecai, Bilshan, Mispereth, Bigvai, Nehum, Baanah. The number of the men of the people of Israel:
8 Zidzukulu za Parosi 2,172
the sons of Parosh, two thousand a hundred and seventy-two;
9 Zidzukulu za Sefatiya 372
the sons of Shephatiah, three hundred seventy and two;
10 Zidzukulu za Ara 652
the sons of Arah, six hundred fifty-two;
11 Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
the sons of Pahath-moab, of the sons of Jeshua and Joab, two thousand and eight hundred and eighteen;
12 Zidzukulu za Elamu 1,254
the sons of Elam, a thousand two hundred fifty-four;
13 Zidzukulu za Zatu 845
the sons of Zattu, eight hundred forty-five;
14 Zidzukulu za Zakai 760
the sons of Zaccai, seven hundred and sixty;
15 Zidzukulu za Binuyi 648
the sons of Binnui, six hundred forty-eight;
16 Zidzukulu za Bebai 628
the sons of Bebai, six hundred twenty-eight;
17 Zidzukulu za Azigadi 2,322
the sons of Azgad, two thousand three hundred twenty-two;
18 Zidzukulu za Adonikamu 667
the sons of Adonikam, six hundred sixty-seven;
19 Zidzukulu za Abigivai 2,067
the sons of Bigvai, two thousand sixty-seven;
20 Zidzukulu za Adini 655
the sons of Adin, six hundred fifty-five;
21 Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
the sons of Ater, of Hezekiah, ninety-eight;
22 Zidzukulu za Hasumu 328
the sons of Hashum, three hundred twenty-eight;
23 Zidzukulu za Bezayi 324
the sons of Bezai, three hundred twenty-four;
24 Zidzukulu za Harifu 112
the sons of Hariph, a hundred and twelve;
25 Zidzukulu za Gibiyoni 95.
the sons of Gibeon, ninety-five;
26 Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
the men of Bethlehem and Netophah, a hundred eighty-eight;
27 Anthu a ku Anatoti 128
the men of Anathoth, a hundred twenty-eight;
28 Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
the men of Beth-azmaveth, forty-two;
29 Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
the men of Kiriath-jearim, Chephirah, and Beeroth, seven hundred forty-three;
30 Anthu a ku Rama ndi Geba 621
the men of Ramah and Geba, six hundred twenty-one;
31 Anthu a ku Mikimasi 122
the men of Michmas, a hundred and twenty-two;
32 Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
the men of Bethel and Ai, a hundred twenty-three;
33 Anthu a ku Nebo winayo 52
the men of the other Nebo, fifty-two;
34 Ana a Elamu wina 1,254
the sons of the other Elam, a thousand two hundred fifty-four;
35 Zidzukulu za Harimu 320
the sons of Harim, three hundred and twenty;
36 Zidzukulu za Yeriko 345
the sons of Jericho, three hundred forty-five;
37 Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
the sons of Lod, Hadid, and Ono, seven hundred twenty-one;
38 Zidzukulu za Senaya 3,930.
the sons of Senaah, three thousand nine hundred and thirty.
39 Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
The priests: the sons of Jedaiah, of the house of Jeshua, nine hundred seventy-three;
40 Zidzukulu za Imeri 1,052
the sons of Immer, a thousand fifty-two;
41 Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
the sons of Pashhur, a thousand two hundred forty-seven;
42 Zidzukulu za Harimu 1,017.
the sons of Harim, a thousand and seventeen.
43 Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
The Levites: the sons of Jeshua, of Kadmiel, of the sons of Hodevah, seventy-four.
44 Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
The singers: the sons of Asaph, a hundred forty-eight.
45 Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
The porters: the sons of Shallum, the sons of Ater, the sons of Talmon, the sons of Akkub, the sons of Hatita, the sons of Shobai, a hundred thirty-eight.
46 Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
The Nethinim: the sons of Ziha, the sons of Hasupha, the sons of Tabbaoth,
47 Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
the sons of Keros, the sons of Sia, the sons of Padon,
48 Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
the sons of Lebana, the sons of Hagaba, the sons of Salmai,
49 Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
the sons of Hanan, the sons of Giddel, the sons of Gahar,
50 Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
the sons of Reaiah, the sons of Rezin, the sons of Nekoda,
51 Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
the sons of Gazzam, the sons of Uzza, the sons of Paseah.
52 Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
The sons of Besai, the sons of Meunim, the sons of Nephushesim,
53 Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
the sons of Bakbuk, the sons of Hakupha, the sons of Harhur,
54 Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
the sons of Bazlith, the sons of Mehida, the sons of Harsha,
55 Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
the sons of Barkos, the sons of Sisera, the sons of Temah,
56 Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
the sons of Neziah, the sons of Hatipha.
57 Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
The sons of Solomon's servants: the sons of Sotai, the sons of Sophereth, the sons of Perida,
58 zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
the sons of Jaala, the sons of Darkon, the sons of Giddel,
59 zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
the sons of Shephatiah, the sons of Hattil, the sons of Pochereth-hazzebaim, the sons of Amon.
60 Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
All the Nethinim and the sons of Solomon's servants, were three hundred ninety-two.
61 Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
And these were those who went up from Tel-melah, Tel-harsha, Cherub, Addon, and Immer, but they could not show their fathers' house, nor their seed, whether they were of Israel:
62 Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
The sons of Delaiah, the sons of Tobiah, the sons of Nekoda, six hundred forty-two.
63 Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
And of the priests: the sons of Hobaiah, the sons of Hakkoz, the sons of Barzillai, who took a wife of the daughters of Barzillai the Gileadite, and was called after their name.
64 Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
These sought their registration among those who were reckoned by genealogy, but it was not found. Therefore they were deemed polluted and put from the priesthood.
65 Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
And the governor said to them that they should not eat of the most holy things till there stood up a priest with Urim and Thummim.
66 Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
The whole assembly together was forty-two thousand three hundred and sixty,
67 Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
besides their men-servants and their maid-servants, of whom there were seven thousand three hundred thirty-seven. And they had two hundred forty-five singing men and singing women.
68 Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
Their horses were seven hundred thirty-six, their mules, two hundred forty-five,
69 Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
their camels, four hundred thirty-five, their donkeys, six thousand seven hundred and twenty.
70 Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
And some from among the heads of fathers gave to the work. The governor gave to the treasury a thousand darics of gold, fifty basins, five hundred and thirty priests' garments.
71 Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
And some of the heads of fathers gave into the treasury of the work twenty thousand darics of gold, and two thousand and two hundred pounds of silver.
72 Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
And that which the rest of the people gave was twenty thousand darics of gold, and two thousand pounds of silver, and sixty-seven priests' garments.
73 Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.
So the priests, and the Levites, and the porters, and the singers, and some of the people, and the Nethinim, and all Israel, dwelt in their cities. And when the seventh month came, the sons of Israel were in their cities.

< Nehemiya 7 >