< Estere 4 >

1 Mordekai atamva zonse zimene zinachitika, anangʼamba zovala zake, navala chiguduli ndi kudzola phulusa, ndipo analowa mu mzinda, akulira mokweza ndi mowawidwa mtima.
Now when Mordecai knew all that was done, Mordecai tore his clothes, and put on sackcloth with ashes, and went out into the midst of the city, and cried with a loud and a bitter cry.
2 Ndipo anapita ndi kuyima pa chipata cha mfumu, chifukwa panalibe wina aliyense amaloledwa kulowa pa chipata cha mfumu atavala chiguduli.
And he came even before the king's gate, for none might enter inside the king's gate clothed with sackcloth.
3 Chigawo chilichonse kumene mawu a mfumu ndi lamulo lake zinafika, kunali maliro akulu pakati pa Ayuda. Iwo ankasala zakudya, kulira mofuwula ndi kumadandaula. Ambiri anavala ziguduli ndi kudzola phulusa.
And in every province, wherever the king's commandment and his decree came, there was great mourning among the Jews, and fasting, and weeping, and wailing, and many lay in sackcloth and ashes.
4 Anamwali otumikira mfumukazi Estere ndi adindo ake ofulidwa atabwera ndi kumuwuza za Mordekai, anavutika kwambiri. Estere anamutumizira zovala kuti avale ndi kuti avule chiguduli chake koma Mordekai sanalole zimenezo.
And Esther's maidens and her chamberlains came and told it to her. And the queen was exceedingly grieved. And she sent raiment to clothe Mordecai, and to take his sackcloth from off him, but he did not receive it.
5 Kenaka Estere anayitana Hataki, mmodzi wa adindo a mfumu ofulidwa amene anayikidwa kuti azimutumikira kuti apite kwa Mordekai kuti akamve chimene chimamuvuta komanso chifukwa chochitira zimenezi.
Then Esther called for Hathach, one of the king's chamberlains whom he had appointed to attend upon her, and charged him to go to Mordecai, to know what this was, and why it was.
6 Choncho Hataki anapita kwa Mordekai ku bwalo la mzinda patsogolo pa chipata cha mfumu.
So Hathach went forth to Mordecai to the broad place of the city, which was before the king's gate.
7 Mordekai anamuwuza zonse zimene zinamuchitikira kuphatikizapo mtengo weniweni wa ndalama zimene Hamani analonjeza kupereka mosungira chuma cha mfumu za anthu amene adzawononge a Yuda.
And Mordecai told him of all that had happened to him, and the exact sum of the money that Haman had promised to pay to the king's treasuries for the Jews to destroy them.
8 Mordekai anamupatsanso imodzi mwa makalata a ulamuliro wonena za chiwembuchi amene anawasindikiza ku Susa kukamuonetsa ndi kumufotokozera zonse Estere. Anamuwuzanso kuti akamudandaulire kuti akapite kwa mfumu kukapempha chifundo ndi kuyidandaulira chifukwa cha anthu a mtundu wake.
Also he gave him the copy of the writing of the decree that was given out in Shushan to destroy them, to show it to Esther, and to declare it to her, and to charge her that she should go in to the king to make supplication to him, and to make request before him for her people.
9 Hataki anabwerera ndi kumufotokozera Estere zimene Mordekai ananena.
And Hathach came and told Esther the words of Mordecai.
10 Ndipo Estere anamutuma Hataki kuti akanene kwa Mordekai kuti,
Then Esther spoke to Hathach, and gave him a message to Mordecai saying,
11 “Atumiki onse amfumu ndi anthu a zigawo za mfumu ankadziwa kuti mwamuna kapena mkazi aliyense akalowa ku bwalo lake la mʼkati mosayitanidwa ndi mfumu pali lamulo limodzi: lamuloli ndi lakuti aphedwe. Zimasintha pokhapokha ngati mfumu iloza munthuyo ndi ndodo yagolide kuti akhale ndi moyo. Koma papita masiku makumi atatu ndisanayitanidwe ndi mfumu.”
All the king's servants, and the people of the king's provinces, know, that whoever, whether man or woman, shall come to the king into the inner court, who is not called, there is one law for him, that he be put to death, except those to whom the king shall hold out the golden scepter that he may live. But I have not been called to come in to the king these thirty days.
12 Tsono Mordekai anawuzidwa mawu a Estere.
And they told Esther's words to Mordecai.
13 Kenaka Mordekai anawawuza kuti akamuyankhe Estere motere: “Usaganize kuti iwe wekha mwa Ayuda onse udzapulumuka chifukwa chakuti uli mʼnyumba ya mfumu.
Then Mordecai bade them return answer to Esther, Think not with thyself that thou shall escape in the king's house more than all the Jews.
14 Pakuti ngati ukhalatu chete nthawi ino, chithandizo ndi chipulumutso cha Ayuda zidzachokera kwina nʼkutheka kuti iwe ndi a pa banja la makolo ako mudzafa. Ndipo adziwa ndani mwina unalowa ufumu chifukwa cha nthawi ngati imeneyi?”
For if thou altogether keep quiet at this time, then relief and deliverance will arise to the Jews from another place, but thou and thy father's house will perish. And who knows whether thou have not come to the kingdom for such a time as this?
15 Pamenepo Estere anatumiza yankho ili kwa Mordekai:
Then Esther bade them return answer to Mordecai,
16 “Pitani, mukasonkhanitse pamodzi Ayuda onse amene ali mu Susa ndipo mundisalire chakudya. Musadye kapena kumwa kwa masiku atatu, usiku ndi usana. Ine ndi anamwali anga onditumikira tidzasala chakudya monga inu. Izi zikachitika, ine ndidzapita kwa mfumu, ngakhale kutero ndikutsutsana ndi lamulo. Ndipo ngati nʼkufa ndife ndithu.”
Go, gather together all the Jews that are present in Shushan, and fast ye for me, and neither eat nor drink three days, night or day. I also and my maidens will fast in like manner. And so I will go in to the king, which is not according to the law. And if I perish, I perish.
17 Choncho Mordekai anapita ndi kuchita monga Estere anamupemphera.
So Mordecai went his way, and did according to all that Esther had commanded him.

< Estere 4 >