< 2 Mbiri 35 >

1 Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
And Josiah kept a Passover to Jehovah in Jerusalem. And they killed the Passover on the fourteenth day of the first month.
2 Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
And he set the priests in their offices, and encouraged them to the service of the house of Jehovah.
3 Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
And he said to the Levites who taught all Israel, who were holy to Jehovah, Put the holy ark in the house which Solomon the son of David king of Israel built. There shall no more be a burden upon your shoulders. Now serve Jehovah your God, and his people Israel.
4 Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
And prepare yourselves after your fathers' houses by your divisions, according to the writing of David king of Israel, and according to the writing of Solomon his son.
5 “Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
And stand in the holy place according to the divisions of the fathers' houses of your brothers the sons of the people, and the portion of a fathers' house of the Levites.
6 Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
And kill the Passover, and sanctify yourselves, and prepare for your brothers, to do according to the word of Jehovah by Moses.
7 Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
And Josiah gave to the sons of the people, of the flock, lambs and kids, all of them for the Passover offerings, to all who were present, to the number of thirty thousand, and also three thousand bullocks; these were of the king's substance.
8 Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
And his rulers gave for a freewill offering to the people, to the priests, and to the Levites. Hilkiah and Zechariah and Jehiel, the rulers of the house of God, gave to the priests for the Passover offerings two thousand and six hundred small cattle, and three hundred oxen.
9 Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
Conaniah also, and Shemaiah and Nethanel, his brothers, and Hashabiah and Jeiel and Jozabad, the chiefs of the Levites, gave to the Levites for the Passover offerings five thousand small cattle, and five hundred oxen.
10 Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
So the service was prepared, and the priests stood in their place, and the Levites by their divisions, according to the king's commandment.
11 Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
And they killed the Passover, and the priests sprinkled the blood by their hand, and the Levites skinned them.
12 Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
And they removed the burnt offerings that they might give them according to the divisions of the fathers' houses of the sons of the people, to offer to Jehovah as it is written in the book of Moses. And so they did with the oxen.
13 Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
And they roasted the Passover with fire according to the ordinance. And the holy offerings they boiled in pots, and in caldrons, and in pans, and carried them quickly to all the sons of the people.
14 Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
And afterward they prepared for themselves, and for the priests, because the priests the sons of Aaron were busy in offering the burnt offerings and the fat until night. Therefore the Levites prepared for themselves, and for the priests the sons of Aaron.
15 Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
And the singers the sons of Asaph were in their place according to the commandment of David, and Asaph, and Heman, and Jeduthun the king's seer. And the porters were at every gate. They did not need to depart from their service, for their brothers the Levites prepared for them.
16 Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
So all the service of Jehovah was prepared the same day, to keep the Passover, and to offer burnt offerings upon the altar of Jehovah, according to the commandment of king Josiah.
17 Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
And the sons of Israel who were present kept the Passover at that time, and the feast of unleavened bread seven days.
18 Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
And there was no Passover like to that kept in Israel from the days of Samuel the prophet. Neither did any of the kings of Israel keep such a Passover as Josiah kept, and the priests, and the Levites, and all Judah and Israel that were present, and the inhabitants of Jerusalem.
19 Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
In the eighteenth year of the reign of Josiah this Passover was kept.
20 Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
After all this, when Josiah had prepared the temple, Neco king of Egypt went up to fight against Carchemish by the Euphrates, and Josiah went out against him.
21 Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
But he sent ambassadors to him, saying, What have I to do with thee, thou king of Judah? I come not against thee this day, but against the house with which I have war, and God has commanded me to make haste. Cease thee from meddling with God, who is with me, that he not destroy thee.
22 Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
Nevertheless Josiah would not turn his face from him, but disguised himself that he might fight with him. And he did not hearken to the words of Neco from the mouth of God, and came to fight in the valley of Megiddo.
23 Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
And the archers shot at king Josiah. And the king said to his servants, Remove me, for I am severely wounded.
24 Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
So his servants took him out of the chariot, and put him in the second chariot that he had, and brought him to Jerusalem. And he died, and was buried in the sepulchers of his fathers. And all Judah and Jerusalem mourned for Josiah.
25 Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
And Jeremiah lamented for Josiah. And all the singing men and singing women spoke of Josiah in their lamentations to this day. And they made them an ordinance in Israel, and, behold, they are written in the lamentations.
26 Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
Now the rest of the acts of Josiah, and his good deeds, according to that which is written in the law of Jehovah,
27 zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
and his acts, first and last, behold, they are written in the book of the kings of Israel and Judah.

< 2 Mbiri 35 >