< Nehemiya 1 >

1 Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
The words of Nehemiah the son of Hacaliah. Now it came to pass in the month Chislev, in the twentieth year, as I was in Shushan the palace,
2 Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
that Hanani, one of my brothers, came, he and certain men out of Judah. And I asked them concerning the Jews who had escaped, that were left of the captivity, and concerning Jerusalem.
3 Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
And they said to me, The remnant who are left of the captivity there in the province are in great affliction and reproach. Also the wall of Jerusalem is broken down, and the gates of it are burned with fire.
4 Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
And it came to pass, when I heard these words, that I sat down and wept, and mourned certain days. And I fasted and prayed before the God of heaven,
5 Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
and said, I beseech thee, O Jehovah, the God of heaven, the great and awesome God, who keeps covenant and loving kindness with those who love him and keep his commandments:
6 Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
Let thine ear now be attentive, and thine eyes open, that thou may hearken to the prayer of thy servant, which I pray before thee at this time, day and night, for the sons of Israel thy servants while I confess the sins of the sons of Israel, which we have sinned against thee. Yea, I and my father's house have sinned.
7 Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
We have dealt very corruptly against thee, and have not kept the commandments, nor the statutes, nor the ordinances, which thou commanded thy servant Moses.
8 “Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
Remember, I beseech thee, the word that thou commanded thy servant Moses, saying, If ye trespass, I will scatter you abroad among the peoples,
9 Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
but if ye return to me, and keep my commandments and do them, though your outcasts were in the outermost part of the heavens, yet I will gather them from there, and will bring them to the place that I have chosen, to cause my name to dwell there.
10 “Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
Now these are thy servants and thy people whom thou have redeemed by thy great power, and by thy strong hand.
11 Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.
O Lord, I beseech thee, let now thine ear be attentive to the prayer of thy servant, and to the prayer of thy servants, who delight to fear thy name, and, I pray thee, prosper thy servant this day, and grant him mercy in the sight of this man. Now I was cupbearer to the king.

< Nehemiya 1 >