< Nahumu 1 >

1 Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
The burden of Nineveh. The book of the vision of Nahum the Elkoshite.
2 Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
Jehovah is a jealous God and avenges. Jehovah avenges and is full of wrath. Jehovah takes vengeance on his adversaries, and he reserves wrath for his enemies.
3 Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
Jehovah is slow to anger, and great in power, and will by no means clear the guilty. Jehovah has his way in the whirlwind and in the storm, and the clouds are the dust of his feet.
4 Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
He rebukes the sea, and makes it dry, and dries up all the rivers. Bashan languishes, and Carmel, and the flower of Lebanon languishes.
5 Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
The mountains quake at him, and the hills melt, and the earth is up heaved at his presence. Yea, the world, and all who dwell therein.
6 Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
Who can stand before his indignation? And who can abide in the fierceness of his anger? His wrath is poured out like fire, and the rocks are broken apart by him.
7 Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
Jehovah is good, a stronghold in the day of trouble, and he knows those who take refuge in him.
8 koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
But with an over running flood he will make a full end of her place, and will pursue his enemies into darkness.
9 Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
What do ye devise against Jehovah? He will make a full end. Affliction shall not rise up the second time.
10 Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
For entangled like thorns, and drunken as with their drink, they are consumed utterly as dry stubble.
11 Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
He has gone forth out of thee, who devises evil against Jehovah, who counsels wickedness.
12 Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
Thus says Jehovah: Though they be in full strength, and likewise many, even so they shall be cut down. And he shall pass away. Though I have afflicted thee, I will afflict thee no more.
13 Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
And now I will break his yoke from off thee, and will burst thy bonds apart.
14 Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
And Jehovah has given commandment concerning thee, that no more of thy name be sown. Out of the house of thy gods I will cut off the graven image and the molten image. I will make thy grave, for thou are vile.
15 Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.
Behold, upon the mountains the feet of him who brings good news, who publishes peace! Keep thy feasts, O Judah. Perform thy vows, for the wicked one shall no more pass through thee. He is utterly cut off.

< Nahumu 1 >