< Mika 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
The word of Jehovah that came to Micah the Morashtite in the days of Jotham, Ahaz, and Hezekiah, kings of Judah, which he saw concerning Samaria and Jerusalem.
2 Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
Hear, ye peoples, all of you. Hearken, O earth, and all who are in it, and let the Lord Jehovah be witness against you, the Lord from his holy temple.
3 Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
For, behold, Jehovah comes forth out of his place, and will come down, and tread upon the high places of the earth.
4 Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
And the mountains shall be melted under him, and the valleys shall be split, as wax before the fire, as waters that are poured down a steep place.
5 Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
All this is for the transgression of Jacob, and for the sins of the house of Israel. What is the transgression of Jacob? Is it not Samaria? And what are the high places of Judah? Are they not Jerusalem?
6 “Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
Therefore I will make Samaria as a heap of the field, and as places for planting vineyards. And I will pour down the stones of it into the valley, and I will uncover the foundations of it.
7 Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
And all her graven images shall be beaten to pieces. And all her wages shall be burned with fire, and I will lay desolate all her idols. For she has gathered them from the wages of a harlot, and to the wage of a harlot they shall return.
8 Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
For this I will lament and wail. I will go stripped and naked. I will make a wailing like the jackals, and a lamentation like the ostriches.
9 Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
For her wounds are incurable. For it has come even to Judah. it reaches to the gate of my people, even to Jerusalem.
10 Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
Tell it not in Gath. Weep not at all. I have rolled myself in the dust at Beth-le-aphrah.
11 Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
Pass away, O inhabitant of Shaphir, in nakedness and shame. The inhabitant of Zaanan has not come forth. The wailing of Beth-ezel shall take from you the stay of it.
12 Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
For the inhabitant of Maroth waits anxiously for good, because evil has come down from Jehovah to the gate of Jerusalem.
13 Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
Bind the chariot to the swift steed, O inhabitant of Lachish. She was the beginning of sin to the daughter of Zion, for the transgressions of Israel were found in thee.
14 Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
Therefore thou shall give a parting gift to Moresheth-gath. The houses of Achzib shall be a deceitful thing to the kings of Israel.
15 Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
I will yet bring to thee, O inhabitant of Mareshah, him who shall possess thee. The glory of Israel shall come even to Adullam.
16 Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.
Make thee bald, and cut off thy hair for the sons of thy delight. Enlarge thy baldness as the vulture, for they have gone into captivity from thee.

< Mika 1 >