< Mika 2 >

1 Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
Woe to those who devise iniquity and work evil upon their beds! When the morning is light they practice it, because it is in the power of their hand.
2 Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
And they covet fields, and seize them, and houses, and take them away. And they oppress a man and his house, even a man and his heritage.
3 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
Therefore thus says Jehovah: Behold, I devise an evil against this family, from which ye shall not remove your necks, nor shall ye walk haughtily, for it is an evil time.
4 Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
In that day they shall take up a taunt against you, and lament with a doleful lamentation. And say, We are utterly ruined. He changes the portion of my people. How he removes it from me! He divides our fields to the rebellious.
5 Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
Therefore thou shall have nobody to cast the line by lot in the assembly of Jehovah.
6 Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
Prophesy ye not, they prophesy. They shall not prophesy to these, so reproaches shall not depart.
7 Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
Shall it be said, O house of Jacob, Is the Spirit of Jehovah restricted? Are these his doings? Do not my words do good to him who walks uprightly?
8 Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
But of late my people have risen up as an enemy. Ye strip off the robe with the garment from those who pass by securely as men turning back from war.
9 Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
Ye cast out the women of my people from their pleasant houses. Ye take away my glory from their young sons forever.
10 Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
Arise ye, and depart, for this is not your resting-place, because of uncleanness that destroys, even with a grievous destruction.
11 Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
If a man walking in a spirit of falsehood lies, saying, I will prophesy to thee of wine and of strong drink, he shall even be the prophet of this people.
12 “Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
I will surely assemble, O Jacob, all of thee. I will surely gather the remnant of Israel. I will put them together as the sheep of Bozrah, as a flock in the midst of their pasture. They shall make great noise because of the multitude of men.
13 Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”
The breaker has gone up before them. They have broken forth and passed on to the gate, and have gone out there. And their king has passed on before them, and Jehovah at the head of them.

< Mika 2 >