< Mika 3 >

1 Ndipo ine ndinati, “Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli. Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,
And I said, Hear, I pray you, ye heads of Jacob, and rulers of the house of Israel. Is it not for you to know justice?
2 inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa; inu amene mumasenda khungu la anthu anga, ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;
Ye who hate the good, and love the evil, who pluck off their skin from off them, and their flesh from off their bones,
3 inu amene mumadya anthu anga, mumasenda khungu lawo ndi kuphwanya mafupa awo; inu amene mumawadula nthulinthuli ngati nyama yokaphika?”
who also eat the flesh of my people, and flay their skin from off them, and break their bones, and chop them in pieces, as for the pot, and as flesh within the caldron.
4 Pamenepo adzalira kwa Yehova, koma Iye sadzawayankha. Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.
Then they shall cry to Jehovah, but he will not answer them. Yea, he will hide his face from them at that time, according as they have wrought evil in their doings.
5 Yehova akuti, “Aneneri amene amasocheretsa anthu anga, ngati munthu wina awapatsa chakudya amamufunira ‘mtendere;’ ngati munthu wina sawapatsa zakudya amamulosera zoyipa.
Thus says Jehovah concerning the prophets who make my people to err, who bite with their teeth, and cry, Peace. And he who does not put into their mouths, they even prepare war against him.
6 Nʼchifukwa chake kudzakuderani, simudzaonanso masomphenya, mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso. Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.
Therefore it shall be night to you, that ye shall have no vision. And it shall be dark to you, that ye shall not divine. And the sun shall go down upon the prophets, and the day shall be black over them.
7 Alosi adzachita manyazi ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa. Onse adzaphimba nkhope zawo chifukwa Mulungu sakuwayankha.”
And the seers shall be put to shame, and the diviners confounded. Yea, they shall all cover their lips, for there is no answer from God.
8 Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu, ndi Mzimu wa Yehova, ndi kulungama, ndi kulimba mtima, kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo, kwa Israeli za tchimo lake.
But as for me, I am full of power by the Spirit of Jehovah, and of judgment, and of might, to declare to Jacob his transgression, and to Israel his sin.
9 Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli, inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama; ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
Hear this, I pray you, ye heads of the house of Jacob, and rulers of the house of Israel, who abhor justice, and pervert all equity.
10 inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi, ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
They build up Zion with blood, and Jerusalem with iniquity.
11 Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze, ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire, ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama. Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti, “Kodi Yehova sali pakati pathu? Palibe tsoka limene lidzatigwere.”
The heads of it judge for a bribe, and the priests of it teach for a wage, and the prophets of it divine for money. Yet they lean upon Jehovah, and say, Is not Jehovah in the midst of us? No evil shall come upon us.
12 Choncho chifukwa cha inu, Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.
Therefore for your sake Zion shall be plowed as a field, and Jerusalem shall become heaps, and the mountain of the house as the high places of a forest.

< Mika 3 >